< Jeremiah 17 >

1 The sin of Judah is inscribed with an iron stylus, engraved with an adamant point, on their minds and on corners of their altars where they worship.
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 Even their children remember to worship at their pagan altars and Asherah poles, set up by the green trees and on the high hills,
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 on my mountain in the fields. I will hand over your wealth and all your valuable possessions as plunder, because of the sin committed on your pagan high places inside your country.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
4 You will have to give up the land I gave you. I will have your enemies make you their slaves in an unfamiliar country for you made my anger blaze, and it will burn forever.
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 This is what the Lord says: Cursed are those who put their confidence in human beings, who trust in human strength and give up relying on the Lord.
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 They will be like a shrub alone in the desert that isn't even aware when good things happen. It just goes on living in the dry desert, in a salt flat that's uninhabited.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 Blessed are those who trust in the Lord, who put their confidence in him.
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
8 They are like trees planted by water, sending out roots toward the stream. They don't panic when it gets hot; their leaves are always green. They don't worry during a time of drought—they go on producing fruit.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 The mind is more deceptive than anything else—it's incurably sick! Who can possibly understand it?
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
10 But I, the Lord, see what people are thinking. I examine their minds, so I can reward them depending on their attitudes and the way they behave.
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 Like a partridge hatching eggs it didn't lay is someone who makes a fortune by cheating others. Their riches will fly away at midday, and in the end they'll look like a fool.
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 Our Temple is a throne of glory, raised up high from the beginning.
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 Lord, you are Israel's hope, anyone who deserts you will be disgraced. Anyone who turns their back on you will vanish like names written in the dust, for they have abandoned the Lord, the source of living water.
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Please heal me, Lord, and I'll be healed; save me, and I'll be saved, for you are the one I praise.
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 See how they keep on saying to me, “Where is the disaster that the Lord's predicted? Is it ever going to happen?”
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 But I haven't been in a hurry to give up being your shepherd. I haven't wanted the time of trouble to come. You know that whatever I said was said in front of you.
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 Please don't be the one who terrifies me! You are my protection in the time of trouble.
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 Bring shame on my persecutors, but not on me. Terrify them, but not me, Let them experience the time of trouble, and smash them to pieces.
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
19 This is what the Lord told me: Go and stand at the main gate of the city, the one used by kings of Judah, and do the same at all the other gates of Jerusalem.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
20 Tell them, Listen to the Lord's message, kings of Judah, and all you people of Judah and Jerusalem who come in through these gates.
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
21 This is what the Lord says: Pay attention, if you value your lives! Don't carry a load on the Sabbath day, and don't bring it through the gates of Jerusalem.
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22 Don't carry a load out of your houses, and don't do any work on the Sabbath day. Keep the Sabbath day holy, just as I ordered your forefathers.
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
23 However, they refused to listen or pay attention. Instead they were stubborn and refused to obey or accept instruction.
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
24 Listen carefully to me, says the Lord, and don't bring any load through the gates of this city on the Sabbath day, and keep the Sabbath day holy, and don't do any work on it.
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
25 Then kings and princes will enter through the gates of this city. They will sit on the throne of David. They will ride in chariots and on horses with their officials, accompanied by the people of Judah and those living in Jerusalem, and this city will be inhabited forever.
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
26 People will come from the towns of Judah and everywhere around Jerusalem, from the land of Benjamin, and from the lowlands the hill country, and the Negev. They will bring burnt offerings and sacrifices, grain offerings and frankincense, and thank offerings to the Lord's Temple.
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
27 But if you refuse to listen to me and keep the Sabbath day holy by not carrying a load while entering the gates of Jerusalem on the Sabbath day, then I will set its gates alight with a fire that can't be put out, and it will burn down Jerusalem's fortresses.
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”

< Jeremiah 17 >