< Jeremiah 1 >
1 These are the words of Jeremiah son of Hilkiah, one of the priests living in Anathoth in the territory of Benjamin.
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 The Lord's message came to Jeremiah beginning in the thirteenth year of the reign of Josiah, son of Amon, king of Judah,
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 and on through the time of Jehoiakim, son of Josiah, king of Judah, up to the fifth month of the eleventh year of Zedekiah, son of Josiah, king of Judah, which was when the people of Jerusalem went into exile.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 The Lord came and told me,
Yehova anayankhula nane kuti,
5 “I knew exactly who you would be before I created you in your mother's womb; I chose you before you were born to be a prophet to the nations.”
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 “Oh no, Lord God!” I replied. “I really don't know how to speak in public because I'm still too young!”
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 “Don't say you're too young,” the Lord told me. “Go to everyone I send you to. Tell them everything I order you to say.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Don't be afraid of them because I'll go with you and I'll look after you. This is the Lord's promise.”
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 The Lord stretched out his hand, touched my mouth, and told me: “Look, I've put my words in your mouth.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Today I've placed you over nations and kingdoms to pull up and tear down, to destroy and demolish, to build and plant.”
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 The Lord's message came to me, asking, “Jeremiah, what can you see?” “I see a twig from an almond tree,” I answered.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 “That's right, because I am watching to make sure what I say happens,” the Lord said.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 The Lord's message came to me again, asking, “What can you see?” “I see a pot that's boiling,” I answered, “and it's tipping in this direction from the north.”
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Then the Lord told me, “Trouble brewing from the north will sweep out over everyone living in the country.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Watch out! I'm going to summon all the nations and kings of the north,” declares the Lord. “Each of these kings will come and set up their thrones right at the entrance of the gates of Jerusalem, and attack all its fortifications and all the towns in Judah.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 I will carry out my sentence against the inhabitants for all their wickedness, because they abandoned me to burn incense to pagan gods, to worship idols they themselves made.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 You need to get yourself ready. You are going to stand before the people and tell them everything that I order you to say. Don't be scared by them, or I will scare you in front of them.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Look! Today I have made you like a fortified city, a pillar of iron, a wall of bronze to stand against the whole country—against the kings of Judah, its officials, its priests, and the people of the country.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 They will fight against you but they won't defeat you, because I'll be there to rescue you,” declares the Lord.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.