< Isaiah 64 >
1 If only you would rip the heavens apart and come down! The mountains would tremble in your presence!
Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
2 In the same way that fire burns wood and makes the water boil, make your reputation known to your enemies, so that nations will tremble in your presence!
Monga momwe moto umatenthera tchire ndiponso kuwiritsa madzi, tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu, ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
3 In the past you did things we weren't anticipating. You came down and the mountains trembled in your presence!
Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere, ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
4 Since the beginning, no one has heard about, no one has paid attention to, and no one has seen any God except you, the one who helps those who place their confidence in you.
Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo kapena kuona Mulungu wina wonga Inu, amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
5 You join with those who are glad, and with those who do what's right and remember to follow your ways. But when we went on sinning, you became angry. How can we be saved if we go on like this?
Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama, amene amakumbukira njira zanu. Koma Inu munakwiya, ife tinapitiriza kuchimwa. Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
6 We've all become unclean, and all the good things we do are like dirty rags. We wither and die like autumn leaves, and our sins, like the wind, blow us away.
Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa, ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo; tonse tafota ngati tsamba, ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
7 There's no one who calls for you or really wants to hold onto you, because you have hidden your face from us and let us drown in our own sins.
Palibe amene amapemphera kwa Inu kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu; pakuti mwatifulatira ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
8 But you, Lord, are our Father. We're the clay, you're the potter. You made us all with your own hands.
Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu. Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba; ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
9 Please limit your anger, Lord, and don't remember our sins forever. Look at us, and see that we are all your people.
Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso musakumbukire machimo athu mpaka muyaya. Chonde, mutiganizire, ife tikupempha, pakuti tonsefe ndi anthu anu.
10 Your holy cities have been turned into a wilderness; Zion has become a desert; yes, even Jerusalem is an abandoned ruin.
Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu; ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
11 Our beautiful, holy Temple where our forefathers praised you has been burned down, and all that we treasured has been destroyed.
Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani, yatenthedwa ndi moto ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
12 In view of all this, are you still going to refuse to help us? Are you going to stay quiet and punish us so severely?
Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza? Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?