< Isaiah 58 >
1 Give a roar from the throat! Don't hold back! Shout out like a trumpet! Announce to my people how rebellious they are; denounce to the descendants of Jacob their sins.
“Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
2 Every day they come to me, pleased to know my ways as if they were a nation that does what is right and follow the laws of their God! They ask me to treat them right; they like to be close to their God.
Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
3 “Didn't you see that we fasted?” they ask. “Didn't you notice how we denied ourselves?” That's because whenever you fast you still do whatever you want, and you treat your workers badly.
Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
4 Can't you see that when you're fasting you quarrel and argue, and end up having a vicious fist-fight? When you fast like this you can't expect your prayers to be heard on high!
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
5 Is this the kind of fast I want when people act out their humility by bowing their heads down like a reed and by lying around in sackcloth and ashes? Is that what you call a fast, a day the Lord appreciates?
Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
6 No, this is the fast I want: set free those who have been unjustly imprisoned, untie the cords of the yoke used to burden people, set free those who are oppressed, and get rid of every form of abuse.
“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
7 Share your food with the hungry, take the poor and homeless into your house. When you see people naked, give them clothes, and don't reject your own relatives.
Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
8 Then your light will shine out like the dawn, and you will be healed quickly; your salvation will go before you, and the glory of the Lord will go behind you.
Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
9 Then when you call, the Lord will answer; when you cry out for help, the Lord will say, “I'm here.” If you get rid of oppression among you, if you stop pointing the finger and slandering others,
Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 if you dedicate yourselves to helping the hungry and give the poor what they need, then your light will shine out in the darkness, and your night will be like the sun at noon.
Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 The Lord will always lead you; he will give you all you need in you in a desolate land; he will make you strong again. You will be like a well-watered garden, like a spring that never runs dry.
Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 Some among you will rebuild the ancient ruins; you will restore generations-old foundations. You will be called the Repairer of the Break in the Wall, the Restorer of Life's Pathways.
Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
13 If you make sure you don't break the Sabbath by doing whatever you please on my holy day, if you say the Sabbath brings you pleasure and the Lord's day is to be honored, and if you honor it by leaving aside your own ways, by not doing whatever you please, and by avoiding everyday chatting,
“Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
14 then you'll find the Lord is the one who truly makes you happy, and I will give you high positions on the earth and give you what I promised to Jacob, your forefather. I, the Lord, have spoken.
mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.