< Isaiah 55 >
1 Come, everyone of you who's thirsty, come and drink the water! You who don't have money, come—you can buy and eat! Come and buy wine and milk—you don't need money; there's no cost!
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Why are you spending money on what isn't food, and why work for something that doesn't satisfy you? Listen carefully to me: eat what is good, and you'll enjoy the very best food.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Come here, and pay attention, so you can truly live. I'm going to make an agreement with you that will last forever, based on the trustworthy love I showed to David.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 See how I made him a witness to the peoples, a leader and commander for them.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 You will call nations you don't even know, and nations who don't know you will come running to you. For the Lord your God, the Holy One of Israel, I made you glorious.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Look for the Lord while you can still find him; call out to him while he's nearby.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Wicked people should change their ways and get rid of even the thought of doing something wrong. They should turn to the Lord so he can be merciful to them. Come back to our God, because he's generous with his forgiveness.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 For your thoughts are not my thoughts; and your ways are not my ways, declares the Lord.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 In the same way the heavens are higher than the earth, my ways are higher than your ways, and my thoughts higher than your thoughts.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 It's like the rain and snow that fall from heaven. They don't go back there until they've watered the earth, making plants grow and flower, providing seeds for the sower and food to eat.
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 In the same way the words I say don't come back to me unfulfilled, they accomplish what I want—they successfully achieve my purpose.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 You will live happily, taught the ways of peace. Mountains and hills will celebrate, singing beside you; and all the trees will clap their hands!
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Cypress trees will grow instead of thorn bushes; myrtle trees will grow instead of brambles. This is to confirm the Lord's reputation—an everlasting sign, never to be destroyed.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”