< Isaiah 26 >

1 At that time, this will be the song that is sung in the land of Judah: “Ours is a strong city! Its walls and defenses are our salvation!
Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
2 Open the gates so the nation who follows the right can come in, the nation that stays faithful.
Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
3 You will keep in complete peace those who keep their minds focused on you, because they trust in you.
Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
4 Trust in the Lord forever, for the Lord God is the eternal Rock.
Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
5 He brings down those who live so high and mighty; he demolishes the proud city with its high walls, bringing it down to the ground, into the dust.
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
6 The poor tread it underfoot; the oppressed walk on top of it.
Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
7 You God, do what is right, and you straighten out the way for those who live right; you smooth out their path.
Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
8 Yes, we follow your instructions, Lord, we put our hope in you. What we most want is to remember you and your wonderful character.
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
9 I look for you in the night; deep inside me I long for you. When your laws are shown to the earth, then the people of the world learn what is right.
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
10 Though grace is shown to the wicked, they don't learn to do right. Even in a country where people do what's right, they continue to do evil and they don't think about how great the Lord is.
Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
11 Lord, you are holding your hand up, but they don't see it. Let them see your passionate commitment for your people, and be embarrassed; may the fire reserved for your enemies destroy them!
Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
12 Lord, you give us peace and prosperity; everything we've achieved you have done for us.
Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
13 Lord our God, there have been other lords besides you who have ruled us, but you are the only one we worship.
Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
14 They are dead, they will not live again; they will not rise from the grave. Lord, you punished them and destroyed them—even wiping out every memory about them.
Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
15 You have made the nation grow, Lord, you have made the nation grow. You have expanded our borders of the land, and we honored you.
Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
16 Lord, when we were suffering we came to you, pouring out our prayers like whispers as you disciplined us.
Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
17 Just as a pregnant woman giving birth tosses about and cries out in pain, that's what we were like in your presence, Lord.
Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
18 However, even though we became pregnant and we tossed about in pain, we gave birth to nothing but air. We did not bring about the salvation of the earth, and the people of the world have not become alive.
Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
19 But those who died in you, Lord, will live! Their bodies will rise again! Wake up, and sing for joy, you people sleeping in the dust, for the dew you receive is like the dew of the morning giving life to those in the grave.
Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
20 My people, go inside your homes and close your doors behind you. Hide there for a little while until the fury has passed.
Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
21 Watch out! The Lord is coming from where he lives to punish the people of the earth for their sins. The earth will reveal the blood that has been shed on it; the earth won't hide those who have been killed any no longer.”
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.

< Isaiah 26 >