< Hosea 1 >

1 The Lord sent a message to Hosea son of Beeri at the time when Uzziah, Jotham, and Ahaz were the kings of Judah, and Jeroboam son of Jehoash was the king of Israel.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 The Lord began speaking through Hosea by telling him, “Go and take a wife who is a prostitute and have children born to a prostitute because those living in this land have committed terrible prostitution by turning away from the Lord.”
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 So Hosea went and married Gomer, the daughter of Diblaim. She became pregnant and bore Hosea a son.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 The Lord told Hosea, “Call him Jezreel, because I am going to punish the house of Jehu for the blood he shed at Jezreel, and I will put an end to the kingdom of Israel.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 On that day I will break Israel's military power in the valley of Jezreel.”
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 Gomer became pregnant again and gave birth to a daughter. The Lord told Hosea, “Call her Lo-ruhamah, because I will no longer love the house of Israel and certainly not forgive them.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 But I will have pity on the house of Judah, and I will save them—but I will not save them by bow or sword or war or horses and riders.”
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 After Gomer had weaned Lo-ruhamah she became pregnant again and gave birth to a son.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 The Lord told Hosea, “Call him Lo-ammi, because you are not my people and I am not your God.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Even so the number of the people of Israel will be like the sand on the seashore that cannot be measured or counted. Then right there at the place where they were told ‘you are not my people’ they will be called ‘the children of the living God.’
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 The people of Israel and the people of Judah will be gathered together and they will choose one leader for themselves and they will take possession of the land, and the day of Jezreel will be great.”
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

< Hosea 1 >