< Genesis 8 >

1 But God hadn't forgotten about Noah and all the wild animals and livestock with him in the ark. God sent a wind to blow over the earth, and the floodwaters started to drop.
Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
2 The subterranean waters were closed off, and the heavy rainfall was stopped.
Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
3 The floodwaters steadily receded from the earth. They had gone down so much that by 150 days after the flood began
Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
4 the ark grounded on the mountains of Ararat. This happened on the seventeenth day of the seventh month.
ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
5 The waters continued to drop so that by the first day of the tenth month the tops of mountains could be seen.
Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
6 Forty days later Noah opened the window he'd made in the ark,
Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
7 and sent a raven out. It flew back and forth until the water on the earth had dried up.
natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
8 Then he sent a dove out to see if the waters had gone down enough to expose dry ground.
Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
9 But the dove couldn't find anywhere to land. So it came back to Noah in the ark because water was still covering the whole earth. He reached out his hand, picked up the dove, and took it back into the ark with him.
Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
10 He waited another seven days and sent the dove out from the ark again.
Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
11 When it came back to him in the evening it had a freshly-picked olive leaf in its beak, so Noah knew the floodwaters were mainly gone from the earth.
Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
12 Again he waited another seven days and sent the dove out again, but this time it didn't return to him.
Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
13 By now Noah was 601, and by the first day of the first month, the floodwaters on the earth were gone. Noah pulled back the ark's covering and saw that the ground was drying out.
Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
14 By the twenty-seventh day of the second month the earth was dry.
Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
15 Then God told Noah,
Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
16 “Leave the ark, you and your wife, your sons and their wives.
“Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
17 Let all the animals go—the birds, the wild animals, the creatures that run along the ground—so that they can breed and increase their numbers on the earth.”
Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
18 So Noah and his wife, his sons and their wives, left the ark.
Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
19 All the animals, all the creatures that run along the ground, all the birds—everything that lives on land—also left, each kind leaving together.
Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
20 Noah built an altar, and sacrificed some of the clean animals and birds as a burnt offering.
Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
21 The Lord accepted the sacrifice, and said to himself, “I won't ever again curse the ground because of human beings, even though every single thought in their minds is evil from childhood. I won't ever destroy all life again as I have just done.
Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
22 As long as the earth exists, seedtime and harvest, cold and heat, summer and winter, day and night, will never come to an end.”
“Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark