< Ezekiel 22 >

1 A message from the Lord came to me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 “So, son of man, are you ready to judge them? Are you ready to judge the people of this city that have caused so much bloodshed? Make them face all the disgusting things they've done,
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 and tell them that this is what the Lord God says: You are a city who has caused your own doom by murdering people within your walls, and by making idols to worship that made you unclean.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 You are guilty of murder, and you have made yourself unclean by the idols you've made. You have shortened your lives—your time is up! That's why other people taunt you—everyone mocks you.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 People far and near will laugh at you, you corrupt city full of confusion!
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Look at how all of your leaders in Israel use their power to murder.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 You despise your parents. You exploit the foreigners who live with you, and you mistreat orphans and widows.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 You detest my holy things and violate my Sabbaths.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 Living among you are people who falsely accuse others in order to put them to death. You also have those who eat religious meals at pagan shrines in the mountains, and commit immoral acts within the city.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 Some of those living in the city have sex with their father's wives or with women during their period.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 You're home to evil men. One does disgusting things with someone else's wife. Another seduces his daughter-in-law, while another rapes his sister, the daughter of his own father.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 Your people take money to murder others. You charge interest and make a profit on loans, and use extortion to get money from your neighbors. You have forgotten all about me, declares the Lord God.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 So watch out! I clap my hands in condemnation at your dishonest profiteering and at all your murders.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Are you going to be so brave, and will you be strong enough to defend yourselves when it comes time for me to deal with you? I, the Lord, have spoken, and I'm going to act.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 I'm going to scatter you among the nations and the different countries. I will put a stop to your unclean acts.
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 For when everyone else sees how you've made yourselves unclean, then you will acknowledge that I am the Lord.”
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 A message from the Lord came to me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
18 “Son of man, the people of Israel have ended up like the impurities left over from refining metal. They're all like copper, tin, iron, and lead in the furnace—they are just the impurities left from refining silver.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 So this is what the Lord God says: Because all of you have ended up like impurities, watch as I collect you together in Jerusalem.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 In the same way a refiner collects silver, copper, iron, lead, and tin and puts them in the blast furnace to melt them with fire, I'm going to collect you in my burning anger, and keep you there until I melt you.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 I'm going to collect you all together and blast you with the fire of my anger, and you'll be melted there in the city.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 Just as silver is melted in a furnace, so you'll be melted in the city. Then you will realize that I, the Lord, have made you experience my anger.”
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 Another message from the Lord came to me, saying,
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 “Son of man, tell the city of Jerusalem, at the time of punishment, you are a country that has not been made clean, a place where no rain has fallen,
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 Her leaders conspire together and it's like watching a roaring lion ripping up its prey. They destroy the people, grab everything that's valuable, and make many more widows in the city.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Her priests pervert my law and make my holy things unclean. They don't distinguish between what is holy and what is ordinary, and they don't separate the clean from the unclean. They forget about my Sabbaths, and they lead people to treat me with no respect.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Her city officials are like wolves ripping up their prey, killing people, destroying lives so they can profit through fraud.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 Her prophets cover up what they do, using false visions as whitewash and prophecies that are lies, saying, ‘This is what the Lord God says,’ when the Lord hasn't said anything.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 The people of this country are extortioners and robbers. They mistreat the poor and those in need and exploit the foreigners, treating them totally unfairly.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 I tried to find one of them repair the wall and defend the gap so when I came I wouldn't destroy it—but I couldn't find anyone.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 So I have let them experience my hostility, burning them up with the fire of my anger. I have made sure they suffer the consequences of what they've done, declares the Lord God.”
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 22 >