< Exodus 6 >
1 But the Lord told Moses, “Now you'll see what I'm going to do to Pharaoh. Using my great strength I will force him to let them go; because of my power he will send them out from his country.”
Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
2 God spoke to Moses and told him, “I am Yahweh!
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
3 I revealed myself as God Almighty to Abraham, to Isaac, and to Jacob, but they didn't know my name, ‘Yahweh.’
Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
4 I also confirmed my solemn agreement with them to give them the land of Canaan, the country where they were living as foreigners.
Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
5 In addition I've heard the groans of the Israelites that the Egyptians are treating as slaves, and I haven't forgotten the agreement I promised them.
Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
6 So tell the Israelites, ‘I am the Lord and I will save you from the forced labor the Egyptians are making you do; I will set you free from being their slaves. I will rescue you using my power and imposing heavy punishments.
“Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
7 I will make you my own people. Then you will know that I am the Lord your God, who rescued you from slavery in Egypt.
Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
8 I will take you to the land that I solemnly promised to give to Abraham, Isaac, and Jacob. I will give it to you to own. I am the Lord!’”
Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
9 Moses explained this to the Israelites but they did not listen to him, because they were so discouraged and because of the hard labor they were forced to do.
Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
10 Then the Lord said to Moses,
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
11 “Go and speak to Pharaoh, king of Egypt. Tell him to let the Israelites leave his country.”
“Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
12 But Moses replied, “Even my own people don't listen to me. Why would Pharaoh listen to me, especially since I'm such a poor speaker?”
Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
13 But the Lord spoke to Moses and Aaron, and told them what to do regarding the people of Israel and Pharaoh, king of Egypt, in order to bring the Israelites out of Egypt.
Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
14 These were the Israelite family heads. The sons of Reuben, the firstborn son of Israel, were Hanok and Pallu, Hezron and Karmi. These were the families of Reuben.
Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
15 The sons of Simeon were Jemuel, Jamin, Ohad, Jachin, Zohar, and Shaul, (the son of a Canaanite woman). These were the families of Simeon.
Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
16 These were the names of the sons of Levi according to their genealogical records: Gershon, Kohath, and Merari. Levi lived for 137 years.
Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
17 The sons of Gershon, by families, were Libni and Shimei.
Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
18 The sons of Kohath were Amram, Izhar, Hebron, and Uzziel. Kohath lived for 133 years.
Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
19 The sons of Merari were Mahli and Mushi. These were the families of the Levites according to their genealogical records.
Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
20 Amram married his father's sister Jochebed, and she had their sons Aaron and Moses. Amram lived for 137 years.
Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
21 The sons of Izhar were Korah, Nepheg, and Zichri.
Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
22 The sons of Uzziel were Mishael, Elzaphan, and Sithri.
Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
23 Aaron married Elisheba, daughter of Amminadab and sister of Nahshon. She had their sons Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
24 The sons of Korah were Assir, Elkanah, and Abiasaph. These were the Korahite families.
Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
25 Eleazar, son of Aaron, married one of the daughters of Putiel, and she had their son Phinehas. These are the ancestors of the Levite families, listed according to their clans. Eleazar son of Aaron married one of the daughters of Putiel, and she gave birth to his son, Phinehas. These are the heads of the Levite families, listed by family.
Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
26 Aaron and Moses mentioned here are the ones the Lord told, “Lead the Israelites out of Egypt, divided up in their respective tribes.”
Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
27 Moses and Aaron were also the ones who went to speak with Pharaoh, king of Egypt, about the Israelites leaving Egypt.
Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
28 When the Lord spoke to Moses in Egypt,
Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
29 he said to him, “I am the Lord. Tell Pharaoh, king of Egypt, all that I tell you.”
anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
30 But Moses replied, “I'm not a good speaker—why would Pharaoh listen to me?”
Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”