< Exodus 22 >

1 “Anyone who steals an ox or a sheep and kills or sells it, he must pay back five oxen for one ox and four sheep for one sheep.
“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.
2 If a thief is discovered breaking into someone's house and is beaten to death, no one shall be guilty of murder.
“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe.
3 But if it happens during daylight, then someone is guilty of murder. A thief must pay everything back that's stolen. If he doesn't have anything, then he must be sold to pay for what was stolen.
Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha. “Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.
4 If what was stolen is a live animal he still has, whether it's an ox, donkey, or sheep, he must pay back double.
“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.
5 If livestock are grazing in a field or vineyard and their owner lets them stray so that they graze in someone else's field, the owner must pay compensation from the best of their own fields or vineyards.
“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.
6 If a fire is started and it spreads to thorn bushes and then burns stacked or standing grain, or even the whole field, the person who started the fire must pay full compensation.
“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.
7 If someone gives his neighbor money or possessions to be kept safe and they are stolen from the neighbor's house, if the thief is caught they must pay back double.
“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.
8 If the thief isn't caught the owner of the house must appear before the judges to find out whether he took his neighbor's property.
Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo.
9 If there's an argument over the ownership of an ox, a donkey, a sheep, a garment, or anything that was lost that someone says, ‘This is mine,’ both parties are to bring their case before the judges. The one whom the judges find in the wrong must pay the other back double.
Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.
10 If someone asks a neighbor to look after a donkey, an ox, a sheep, or any other animal, but it dies or is injured or is stolen without anybody noticing,
“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona,
11 then an oath must be taken before the Lord to decide if the neighbor has taken the owner's property. The owner must accept the oath and not demand compensation.
ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu.
12 However, if the animal really was stolen from the neighbor, he must compensate the owner.
Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.
13 If it was killed and torn to pieces by a wild animal, the neighbor shall present the carcass as evidence and does not need to pay compensation.
Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.
14 If someone borrows a neighbor's animal and it's injured or dies while its owner is not present, they must pay compensation in full.
“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.
15 If the owner was present, no compensation is to be paid. If the animal was hired, only the hire charge needs to be paid.
Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.
16 If a man seduces a virgin who is not engaged to be married and sleeps with her, he must pay the full bride-price for her to become his wife.
“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake.
17 If her father adamantly refuses to give her to him, the man still must pay the same amount as the bride-price for a virgin.
Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.
18 You must not allow a woman who practices witchcraft to live.
“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.
19 Anyone who has sex with an animal must be executed.
“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.
20 Anyone who sacrifices to any other god than the Lord must be set apart and executed.
“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.
21 You must not exploit or mistreat a foreigner. Remember that you yourselves were once foreigners in Egypt.
“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.
22 You must not take advantage of any widow or orphan.
“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye.
23 If you mistreat them, and they call out to me for help, I will definitely respond to their cry.
Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo.
24 I will become angry, and I will kill you with the sword. Your wives will become widows and your children will be fatherless.
Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.
25 If you lend money to any of my people because they're poor, you must not behave as a moneylender to them. You must not charge them any interest.
“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja.
26 If you require your neighbor's cloak as security for a loan, you must return it to him by sunset,
Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe
27 because it's the only clothing he has for his body. What would he sleep in otherwise? If he calls out to me for help, I will listen, for I am considerate.
chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.
28 You must not despise God or curse your people's leader.
“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.
29 You must not hold onto the required offerings of your produce, olive oil, and wine. You must give me the firstborn of your sons.
“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka. “Mundipatse ana anu achisamba aamuna.
30 You must also give me the firstborn of your cattle, sheep, and goats. They can stay with their mothers for their first seven days, but give them to me on the eighth day.
Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.
31 You are to be holy people to me. You must not eat any animal carcass that you find in the countryside that has been killed by wild animals. Throw it to the dogs to eat.”
“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”

< Exodus 22 >