< Deuteronomy 28 >

1 If you truly obey what the Lord your God tells you, and carefully follow all his commandments that I'm giving you today, then the Lord your God will place you high above all the nations of the earth.
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 You will have all the following blessings and even more, if you do what the Lord your God says.
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 You will be blessed when you're in the town; you will be blessed when you're in the countryside.
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 You will be blessed with many children. You will be blessed with good harvests. You will be blessed with livestock—your cattle will have many calves, and your sheep will have many lambs.
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 You will be blessed with plenty of bread.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 You will be blessed wherever you go and in everything you do.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 The Lord will defeat the enemies who come to attack you. They will come at you from one direction, but they will scatter seven different ways.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 The Lord will bless your income and everything you do. The Lord your God will bless you in the country he is giving you.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 The Lord will make you his holy people, just as he promised you, if you obey the Lord your God's commandments and follow his ways.
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 Then everyone on earth will see that the Lord has chosen you to be his, and they will be afraid of you.
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 The Lord will make you very prosperous. You will have many children, your livestock will produce plenty of young, and your land will grow good harvests—all this in the country the Lord promised your forefathers he would give you.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 The Lord will provide rain for your land at the right time from his heavenly storehouse to bless all your work growing crops. You will lend money to many nations but you won't need to borrow from any of them.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 The Lord will put you in first place, not the last. You will only go up, never down, as long as you listen to and follow carefully the commandments of the Lord your God that I'm giving you today.
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 Don't deviate from any of my instructions today. Don't go and worship other gods.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 But if you don't obey the Lord your God by following carefully all his commandments and regulations I'm giving you today, then you will experience all the following curses and more:
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 You will be cursed when you're in the town; you will be cursed when you're in the countryside.
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 You will be cursed by not having bread.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 You will be cursed by not having children, and by not having good harvests, and by your cattle not having calves, and your sheep not having lambs.
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 You will be cursed wherever you go and in everything you do.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 The Lord will send you curses, making you confused and frustrated in everything you do, until you are brought down and die quickly because of the evil that you've done by abandoning him.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 The Lord will give you infectious diseases until he has wiped you out from the country you are entering town.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 Then Lord will hit you with sickness that makes you waste away, with a severe fever and swelling like you're burning up, while your crops are damaged by drought and blight and mildew. These will attack you until you die.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 The sky above you will be like bronze, and the earth beneath you will be like iron.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 The Lord will change the rain of your land into dust and sand; it will fall from the sky on you until you're destroyed.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 The Lord will have your enemies defeat you. You will attack them from one direction, but you will scatter seven different ways. Everyone on earth will be horrified at what happens to you.
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 Your dead bodies will be food for birds of prey and wild animals, and there won't be anyone to scare them away.
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 The Lord will give you boils like he did to the Egyptians, with swellings and scabs and skin rashes that can't be cured.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 The Lord will send you mad and make you blind and confused,
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 so that even at noon you will be groping around like a blind man in the dark. You won't be successful in what you do. You'll be persecuted and robbed the whole time, and no one will come and save you.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 You will be engaged to marry a woman, but another man will sleep with her. You will build a house but you won't live in it. You will plant a vineyard but won't benefit from any harvest.
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 Your ox will be slaughtered right in front of you, but you won't eat any of it. Your donkey will be taken away and won't be returned to you. Your sheep will be taken by your enemies, and no one will come and save you.
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 Your sons and daughters will be taken away as slaves to other nations while you watch, and you'll wear your eyes out crying over them, but there won't be anything you can do about it.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 A foreign nation you've never heard of will eat all the crops you worked so hard to grow. You will be continually persecuted and downtrodden.
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 What you see will drive you mad.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 The Lord will give you painful boils that can't be cured on your knees and thighs, in fact from head to toe.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 The Lord will exile you and your chosen king you to a foreign nation that neither you nor your forefathers had ever heard of. There you will worship other gods, idols made of wood and stone.
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 You will be something that horrifies all the nations where you've been exiled by the Lord. They will laugh at you and ridicule you.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 You will sow a lot of seed in the field, but harvest very little because the locusts will destroy it.
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 You will plant and vineyards and care for them, but you won't harvest the grapes or drink the wine, because they'll be eaten by maggots.
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 You will have olive trees all over the country but you won't have any olive oil to use, because the olives will drop early from the trees.
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 You will have sons and daughters, but you won't have them for long, because they will be taken off into captivity as slaves.
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 Locust swarms will destroy all your trees and crops.
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 Foreigners who live with you will rise higher and higher in status above you, while you sink lower and lower.
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 They will lend to you, but you will not lend to them. They will be the first, and you will be the last.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 All these curses will come down on you. They will chase after you and attack you until you die because you did not obey the Lord your God and keep the commandments and regulations he gave you.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 They will be lasting evidence, visible signs of what happened to you and your descendants.
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 Because you did not serve the Lord your God with happiness and with a joyful attitude,
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 you will serve your enemies that the Lord sends to attack you with hunger, thirst, nakedness, and poverty. He will tie an iron yoke on your neck until he has destroyed you.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 The Lord will bring a nation to attack you from a long way off, from the ends of the earth. They will swoop down upon you like an eagle, this nation whose language you won't understand.
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 They are a ruthless nation who don't respect for the old and have no mercy on the young.
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 They will eat your lambs and calves and the crops you've grown until you are destroyed. They won't leave you any grain or new wine or olive oil, no calves from your herds or lambs from your flocks, so you'll die of starvation.
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 They will besiege all the towns in your country, until the high, fortified walls that you trust in have fallen. They will besiege all your towns in your country that the Lord your God has given you.
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 You'll end up eating your children, the flesh of the sons and daughters the Lord your God gave you, because of the siege and the suffering that your enemy will cause you.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 The kindest and most sensitive man among you will refuse to share his food with his brother, the wife he loves, and those of his own children who are left.
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 He will refuse to share with any of them the flesh of his children that he's forced to eat because he doesn't have anything else because of the siege and suffering your enemy has caused you in all your towns.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 The kindest and most sensitive woman among you, so kind and sensitive she wouldn't ever go barefoot on the ground, will refuse to share her food, a baby and its afterbirth, with the husband she loves and her own son and daughter.
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 She will even secretly eat her the babies she gives birth to and the afterbirth, since she doesn't have anything else because of the siege and suffering your enemy has caused you in all your towns,
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 If you don't carefully observe all these laws written down in this book so that you may show respect for this glorious and awesome Lord your God,
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 he will bring down on you and your descendants unbelievable disasters, intense and long-lasting diseases, and terrible and incurable sicknesses.
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 He will give you all the diseases you were terrified of in Egypt, and they will stay with you.
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 The Lord will also give you every sickness and disease, even those not recorded in this Book of the Law, until you are destroyed.
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 You who grew as numerous as the stars in the sky will end up as only a few, because you would not obey what Lord your God told you.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 In the same way as he wanted to make you prosperous and increase in number, so now he will wipe you out and destroy you. You will be uprooted from the country you are going in to own.
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 The Lord will scatter you among the nations all over the earth, and there you will worship other gods, gods made of wood and stone, which you and your fathers had never heard of.
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 You won't find any place to rest among those nations, no place of your own. The Lord will make you anxious, with failing eyesight and a mind full of despair.
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 You will see your life hanging in the balance as you doubt. You will be afraid day and night, terrified you won't survive.
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 In the morning you'll say, “I wish it was evening!” and in the evening you'll say, “I wish it was morning!” because you're so frightened by the terrifying things you see.
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 The Lord will send you back to Egypt in ships to a place that I said you weren't ever meant to see again. You will put yourselves on sale there to your enemies as male and female slaves, but nobody will want to buy you.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< Deuteronomy 28 >