< Deuteronomy 13 >

1 Maybe a prophet or someone who has dreams about the future comes along and gives you a prediction you about some sign or miracle,
Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa,
2 and the sign or wonder does happens. If after that they tell you, “Let's follow other gods that you don't know, and let's worship them,”
chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe),
3 then you must not listen to what that prophet or dreamer has to say because the Lord your God is trying to find out whether you really love him with all your mind and with all your being.
musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
4 You are to follow the Lord your God and respect him. Keep his commandments and do what he says; worship him and hold onto him.
Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo.
5 These kinds of prophet or dreamer must be executed, because they have promoted rebellion against the Lord your God, who led you out of Egypt and rescued you from the prison-house of slavery. They have tried to lead you from the way that the Lord your God has ordered you to follow. You must eliminate the evil among you.
Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.
6 Even if your own brother, or your son or daughter, or the wife you love, or your best friend secretly encourages you, saying, “Let's go and worship other gods” unfamiliar to you and your forefathers,
Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe,
7 the gods of your pagan nation neighbors, whether they love close by or far away in any direction,
milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi),
8 don't give into them or listen to them. Show them no mercy. Don't spare them or protect them.
musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza.
9 No, you absolutely must kill them! You start killing them, and then have everyone else help.
Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse.
10 Stone the person to death for trying lead you away from the Lord your God, who led you out of Egypt, out of the prison-house of slavery.
Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo.
11 Then every Israelite will hear about it and be afraid, and won't ever do such an evil thing among you.
Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.
12 It may happen that once you're living in the towns the Lord your God is giving you, you hear
Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo,
13 that evil people have taken over in one of your towns and have led the people there astray, telling them, “Let's go and worship other gods” that you don't know.
kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe),
14 If this does happen you need to make a full investigation, inquiring about the facts and interrogating witnesses. If it's proved beyond doubt that this awful sin has actually been committed among you,
mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu,
15 then you have to kill the people living in that town with the sword. Set apart for destruction its people and its livestock.
muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe.
16 You must pile up all the people's possessions in the middle of the public square, and completely burn the town and everything in it as a complete burnt offering to the Lord your God. The town must remain a heap of ruins forever. It must never be rebuilt.
Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso.
17 Don't take for yourselves anything that has been set apart for destruction so that the Lord won't be angry any more. He will be merciful to you, showing you compassion, and giving you many descendants as he promised to your forefathers,
Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu,
18 because you are obeying the Lord your God, keeping all his commandments that I'm giving you today, and doing what is right in the sight of the Lord your God.
chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.

< Deuteronomy 13 >