< 2 Samuel 8 >

1 Sometime after this, David attacked and subdued the Philistines, taking Metheg-ammah from the them.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 David also defeated the Moabites. He made them lie down on the ground, and he measured them with a length of cord. He measured two lengths for those to be killed, and one cord length for those to be allowed to live. So he made them subject to him and required them to pay taxes.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 David also defeated Hadadezer, son of Rehob, king of Zobah, as he tried to enforce his control along the Euphrates River.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 David captured from him 1,000 chariots, 7,000 charioteers, and 20,000 foot soldiers. David hamstrung all the chariot horses—except he saved enough for 100 chariots.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 When the Arameans of Damascus came to help King Hadadezer of Zobah, David killed twenty-two thousand of them.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 He placed garrisons in Aramean kingdom with its capital in Damascus, and made the Arameans subject to him and required them to pay taxes. The Lord gave David victories wherever he went.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 David took the shields of gold that belonged to Hadadezer's officers and brought them to Jerusalem.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 King David also took a large quantity of bronze from Betah and Berothai, towns that had belonged to Hadadezer.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 When Tou, king of Hamath, learned that David had destroyed the entire army of Hadadezer, king of Zobah,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 he sent his son Joram to David to make friends with him and to congratulate him on his victory in battle over Hadadezer. Tou and Hadadezer had often been at war. Joram brought all kinds of gifts of gold, silver, and bronze.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 King David dedicated these gifts to the Lord, along with the silver and gold he had taken from all the nations he had subdued:
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 Edom, Moab, the Ammonites, the Philistines, and Amalekites; as well as the plunder taken from Hadadezer, son of Rehob, king of Zobah.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 David also made a name for himself when he came back after defeating eighteen thousand Edomites in the Valley of Salt.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 He placed garrisons all through Edom, and all the Edomites became subject to David. The Lord gave David victories wherever he went.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 David ruled over all Israel. He did what was fair and right for all his people.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Joab, son of Zeruiah, was the army commander, and Jehoshaphat, son of Ahilud, kept the official records.
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 Zadok, son of Ahitub, and Ahimelech, son of Abiathar, were priests, while Seraiah was the secretary.
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 Benaiah, son of Jehoiada was in charge of the Cherethites and Pelethites; and David's sons were priests.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

< 2 Samuel 8 >