< 1 Kings 13 >

1 The Lord ordered a man of God from Judah to go to Bethel. He arrived just as Jeroboam was standing beside the altar about to present a burnt offering.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 He shouted out the Lord's condemnation of the altar: “Altar, altar, this is what the Lord says. A son will be born to the house of David. His name will be Josiah, and on you he will sacrifice the priests of the high places who burn offerings on you, and human bones will be burned on you.”
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 The same day the man of God gave a sign, saying, “This is the sign to prove that the Lord has spoken. Look! The altar will be split apart, and the ashes on it will spill out.”
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 When King Jeroboam heard the condemnation the man of God had shouted out against the altar in Bethel, he pointed his hand at him and said, “Arrest him!” But the hand the king had pointed at him had become paralyzed and he couldn't draw it back.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 The altar split apart, and the ashes spilled out from it, fulfilling the sign that the man of God had given from the Lord.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 Then the king said to the man of God, “Please plead with the Lord your God—pray for me that I may have my hand back!” The man of God pleaded with the Lord, and the king was given back the use of his hand as it was before.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 Then the king said to the man of God, “Come to my home and have a meal so I can give you a present.”
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 But the man of God told the king, “Even if you gave me half of everything you own, I still wouldn't go with you. In fact I refuse to eat or drink anything in this place.
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 The Lord ordered me not to eat or drink anything, and not to return by the way I came.”
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 So he went a different way—he did not return the way he had come to Bethel.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 It so happened that an old prophet lived in Bethel. His sons came and told him everything the man of God had done that day in Bethel. They also told their father what the man had said to the king.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 “Which way did he go?” their father asked them. So his sons showed him the way taken by the man of God from Judah.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 “Saddle up a donkey for me,” he told his sons. They saddled up a donkey and he got on.
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 He rode after the man of God and found him sitting under an oak tree. “Are you the man of God who came from Judah?” he asked him. “Yes I am,” the man replied.
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 “Come home with me and have something to eat,” he told him.
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 “I can't turn around and go with you, and I won't eat or drink with you in this place,” the man of God replied.
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 “The Lord ordered me, saying ‘You must not eat or drink anything there, or return by the way you came.’”
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 But the old prophet told him, “I am also a prophet, just like you. An angel told me God said, ‘Take him home with you so that he can have something to eat and drink’” But he was lying to him.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 So the man of God went back with him, and ate and drank in his house.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 As they were sitting at the table, a message from the Lord came to the prophet who had brought him back.
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 He called out to the man of God who had come from Judah, “This is what the Lord says: Because you have disobeyed the word of the Lord and have not followed the orders that the Lord your God gave you,
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 instead you went back and ate and drank in the place where he told you not to, your body will not be buried in the tomb of your fathers.”
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 After the man of God had finished eating and drinking, the prophet who had brought him back saddled his own donkey for him.
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 But as he went on his way a lion came across him on the road and killed him. His body was left lying in the road, with both the donkey and the lion standing beside it.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 Some passers-by saw the body lying in the road with the lion standing beside it, so they went and let people know about it in the town where the old prophet lived.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 When the old prophet who had led the other astray heard what had happened, he said, “It's the man of God who disobeyed the Lord's orders. That's why the Lord put him in the path of the lion, and it has mauled him and killed him, just as the Lord told him would happen.”
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 The prophet told his sons, “Saddle up a donkey for me.” So they saddled a donkey,
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 and he went and found the body. It was still lying in the road, with the donkey and the lion standing beside it. The lion had not eaten the body or attacked the donkey.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 The prophet picked up the body of the man of God, placed it on the donkey, and brought it back to his own town to mourn over him and bury him.
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 He laid the body in his own tomb, and they mourned over him, crying, “My poor brother!”
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 After he'd buried him, he told his sons, “When I die, bury me in the grave where the man of God is buried. Lay my bones beside his bones.
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 For the message from the Lord that he gave in condemnation against the altar in Bethel, and against all the shrines on the high places in the towns of Samaria, will definitely happen.”
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 But even after all this, Jeroboam did not change his evil ways. He went on choosing priests from all kinds of people. He appointed anyone who wanted to be a priest of the high places.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 This was because of this sin that the house of Jeroboam was wiped out, completely destroyed from the face of the earth.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Kings 13 >