< 1 Chronicles 23 >

1 When David was old, having lived a long life, he made his son Solomon king of Israel.
Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
2 He also summoned all the leaders of Israel, the priests, and the Levites.
Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
3 The Levites over thirty years old were counted, and there was 38,000 in total.
Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
4 “Of these 24,000 will be in charge of the work of the house of the LORD, while 6,000 will be officers and judges,” David instructed.
Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
5 “And 4,000 will be gatekeepers, while 4,000 will praise the Lord using the musical instruments I have provided for praise worship.”
Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
6 David divided them into sections corresponding to the sons of Levi: Gershon, Kohath, and Merari.
Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
7 The sons of Gershon: Ladan and Shimei.
Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
8 The sons of Ladan: Jehiel (chief), and Zetham, and Joel, three in total.
Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
9 The sons of Shimei: Shelomoth, Haziel, and Haran, three in total. These were the leaders of the families of Ladan.
Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
10 The sons of Shimei: Jahath, Zizah, Jeush, and Beriah—four in total.
Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
11 Jahath (chief), and Zizah (second); but because Jeush and Beriah did not have many sons they were counted as a single family.
Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
12 The sons of Kohath: Amram, Izhar, Hebron, and Uzziel—a total of four.
Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
13 The sons of Amram: Aaron and Moses. Aaron was dedicated to service with the most holy things, that he and his sons should always present offerings to the Lord, and minister before him, and give blessings in his name forever.
Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
14 As for Moses, the man of God, his sons were included with the tribe of Levi.
Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
15 The sons of Moses: Gershom and Eliezer.
Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
16 The sons of Gershom: Shebuel (chief).
Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
17 The sons of Eliezer: Rehabiah (chief). Eliezer had no other sons, but Rehabiah had many sons.
Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
18 The sons of Izhar: Shelomith (chief).
Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
19 The sons of Hebron: Jeriah (chief), Amariah (second), Jahaziel (third), and Jekameam (fourth).
Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
20 The sons of Uzziel: Micah (chief) and Isshiah (second).
Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
21 The sons of Merari: Mahli and Mushi. The sons of Mahli: Eleazar and Kish.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
22 Eleazar died without having sons, only daughters. Their cousins, the sons of Kish, married them.
Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
23 The sons of Mushi: Mahli, Eder, and Jeremoth—three in total.
Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
24 These were the descendants of Levi by family, the heads of families chiefs listed individually by name—those twenty years of age or more who served in the house of the Lord.
Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
25 For David said, “The Lord, the God of Israel, has given peace to his people, and he will live in Jerusalem forever.
Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
26 So the Levites don't need to carry the Tent any longer, or anything needed for its service.”
sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
27 In accordance with David's final instructions, Levites twenty years of age or more were counted.
Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
28 Their assignment was to help the descendants of Aaron with the service of the house of the Lord They were responsible for the courtyards and rooms, for cleansing all the holy things, and the work of the service of the house of God.
Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
29 They were also responsible for the showbread that was placed on the table, the special flour for the grain offerings, the unleavened bread, the baking, the mixing, and dealing with all amounts and measurements.
Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
30 They also had to stand every morning to give thanks and praise to the Lord, and do the same in the evening,
Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
31 and whenever burnt offerings were presented to the Lord whether on Sabbaths, new moons, and feast days. They were to serve regularly before the Lord according to the number required for them.
ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
32 So the Levites were to carry out the responsibility of caring for the Tent of Meeting and the sanctuary, and with their brothers the descendants of Aaron, they served the house of the Lord.
Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.

< 1 Chronicles 23 >