< Zechariah 13 >
1 In that day there shall be a fountain open to the house of David, and to the inhabitants of Jerusalem: for the washing of the sinner, and of the unclean woman.
“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 And it shall come to pass in that day, saith the Lord of hosts, that I will destroy the names of idols out of the earth, and they shall be remembered no more: and I will take away the false prophets, and the unclean spirit out of the earth.
“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
3 And it shall come to pass, that when any man shall prophesy any more, his father and his mother that brought him into the world, shall say to him: Thou shalt not live: because thou best spoken a lie in the name of the Lord. And his father, and his mother, his parents, shall thrust him through, when he shall prophesy.
Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 And it shall come to pass in that day, that the prophets shall be confounded, every one by his own vision, when he shall prophesy, neither shall they be clad with a garment of sackcloth, to deceive:
“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
5 But he shall say: I am no prophet, I am a husbandman: for Adam is my example from my youth.
Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
6 And they shall say to him: What are these wounds in the midst of thy hands? And he shall say: With these I was wounded in the house of them that loved me.
Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
7 Awake, O sword, against my shepherd, and against the man that cleaveth to me, saith the Lord of hosts: strike the shepherd, and the sheep shall be scattered: and I will turn my hand to the little ones.
“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 And there shall be in all the earth, saith the Lord, two parts in it shall be scattered, and shall perish: but the third part shall be left therein.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 And I will bring the third part through the fire, and will refine them as silver is refined: and I will try them as gold is tried. They shall call on my name, and I will hear them. I will say: Thou art my people: and they shall say: The Lord is my God.
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”