< Psalms 67 >
1 Unto the end, in, hymns, a psalm of a canticle for David. May God have mercy on us, and bless us: may he cause the light of his countenance to shine upon us, and may he have mercy on us.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 That we may know thy way upon earth: thy salvation in all nations.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Let people confess to thee, O God: let all people give praise to thee.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Let the nations be glad and rejoice: for thou judgest the people with justice, and directest the nations upon earth.
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Let the people, O God, confess to thee: let all the people give praise to thee:
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 The earth hath yielded her fruit. May God, our God bless us,
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 May God bless us: and all the ends of the earth fear him.
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.