< Psalms 55 >

1 Unto the end, in verses, understanding for David. Hear, O God, my prayer, and despise not my supplication:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 Be attentive to me and hear me. I am grieved in my exercise; and am troubled,
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 At the voice of the enemy, and at the tribulation of the sinner. For they have cast iniquities upon me: and in wrath they were troublesome to me.
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 My heart is troubled within me: and the fear of death is fallen upon me.
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 Fear and trembling are come upon me: and darkness hath covered me.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 And I said: Who will give me wings like a dove, and I will fly and be at rest?
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Lo, I have gone far off flying away; and I abode in the wilderness.
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 I waited for him that hath saved me from pusillanimity of spirit, and a storm.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Cast down, O Lord, and divide their tongues; for I have seen iniquity and contradiction in the city.
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Day and night shall iniquity surround it upon its walls: and in the midst thereof are labour,
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 And injustice. And usury and deceit have not departed from its streets.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 For if my enemy had reviled me, I would verily have borne with it. And if he that hated me had spoken great things against me, I would perhaps have hidden myself from him.
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 But thou a man of one mind, my guide, and my familiar,
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Who didst take sweetmeats together with me: in the house of God we walked with consent.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Let death come upon them, and let them go down alive into hell. For there is wickedness in their dwellings: in the midst of them. (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 But I have cried to God: and the Lord will save me.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Evening and morning, and at noon I will speak and declare: and he shall hear my voice.
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 He shall redeem my soul in peace from them that draw near to me: for among many they were with me.
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 God shall hear, and the Eternal shall humble them. For there is no change with them, and they have not feared God:
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 He hath stretched forth his hand to repay. They have defiled his covenant,
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 They are divided by the wrath Of his countenance, and his heart hath drawn near. His words are smoother than oil, and the same are darts.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Cast thy care upon the Lord, and he shall sustain thee: he shall not suffer the just to waver for ever.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 But thou, O God, shalt bring them down into the pit of destruction. Bloody and deceitful men shall not live out half their days; but I will trust in thee, O Lord.
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< Psalms 55 >