< Psalms 4 >
1 Unto the end, in verses. A psalm for David. When I called upon him, the God of my justice heard me: when I was in distress, thou hast enlarged me. Have mercy on me: and hear my prayer.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 O ye sons of men, how long will you be dull of heart? why do you love vanity, and seek after lying?
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 Know ye also that the Lord hath made his holy one wonderful: the Lord will hear me when I shall cry unto him.
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Be angry, and sin not: the things you say in your hearts, be sorry for them upon your beds.
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 Offer up the sacrifice of justice, and trust in the Lord: many say, Who sheweth us good things?
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 The light of thy countenance O Lord, is signed upon us: thou hast given gladness in my heart.
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 By the fruit of their corn, their wine and oil, they are multiplied.
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 In peace in the selfsame I will sleep, and I will rest: For thou, O Lord, singularly hast settled me in hope.
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.