< Psalms 33 >

1 A psalm for David. Rejoice in the Lord, O ye just: praise becometh the upright.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Give praise to the Lord on the harp; sing to him with the psaltery, the instrument of ten strings.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Sing to him a new canticle, sing well unto him with a loud noise.
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 For the word of the Lord is right, and all his works are done with faithfulness.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 He loveth mercy and judgment; the earth is full of the mercy of the Lord.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 By the word of the Lord the heavens were established; and all the power of them by the spirit of his mouth:
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Gathering together the waters of the sea, as in a vessel; laying up the depths in storehouses.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Let all the earth fear the Lord, and let all the inhabitants of the world be in awe of him.
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 For he spoke and they were made: he commanded and they were created.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 The Lord bringeth to naught the counsels of nations; and he rejecteth the devices of people, and casteth away the counsels of princes.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 But the counsel of the Lord standeth for ever: the thoughts of his heart to all generations.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Blessed is the nation whose God is the Lord: the people whom he hath chosen for his inheritance.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 The Lord hath looked from heaven: he hath beheld all the sons of men.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 From his habitation which he hath prepared, he hath looked upon all that dwell on the earth.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 He who hath made the hearts of every one of them: who understandeth all their works.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 The king is not saved by a great army: nor shall the giant be saved by his own great strength.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Vain is the horse for safety: neither shall he be saved by the abundance of his strength.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Behold the eyes of the Lord are on them that fear him: and on them that hope in his mercy.
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 To deliver their souls from death; and feed them in famine.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Our soul waiteth for the Lord: for he is our helper and protector.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 For in him our heart shall rejoice: and in his holy name we have trusted.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Let thy mercy, O Lord, be upon us, as we have hoped in thee.
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< Psalms 33 >