< Psalms 118 >
1 Give praise to Lord, for he is good: for his mercy endureth for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Let Israel now say that he is good: that his mercy endureth for ever.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Let the house of Aaron now say, that his mercy endureth for ever.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Let them that fear the Lord now say, that his mercy endureth for ever.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 In my trouble I called upon the Lord: and the Lord heard me, and enlarged me.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 The Lord is my helper, I will not fear what man can do unto me.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 The Lord is my helper: and I will look over my enemies.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is good to confide in the Lord, rather than to have confidence in man.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is good to trust in the Lord, rather than to trust in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations compassed me about; and in the name of the Lord I have been revenged on them.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Surrounding me they compassed me about: and in the name of the Lord I have been revenged on them.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They surrounded me like bees, and they burned like fire among thorns: and in the name of the Lord I was revenged on them.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Being pushed I was overturned that I might fall: but the Lord supported me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 The Lord is my strength and my praise: and he is become my salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The voice of rejoicing and of salvation is in the tabernacles of the just.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of the Lord hath wrought strength: the right hand of the Lord hath exulted me: the right hand of the Lord hath wrought strength.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I shall not die, but live: and shall declare the works of the Lord.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 The Lord chastising hath chastised me: but he hath not delivered me over to death.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open ye to me the gates of justice: I will go into them, and give praise to the Lord.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This is the gate of the Lord, the just shall enter into it.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I will give glory to thee because thou hast heard me: and art become my salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 The stone which the builders rejected; the same is become the head of the corner.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This is the Lord’s doing: and it is wonderful in our eyes.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the day which the Lord hath made: let us be glad and rejoice therein.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 O Lord, save me: O Lord, give good success.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed be he that cometh in the name Lord. We have blessed you out of the house of the Lord.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 The Lord is God, and he hath shone upon us. Appoint a solemn day, with shady boughs, even to the horn of the alter.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Thou art my God, and I will praise thee: thou art my God, and I will exalt thee. I will praise thee, because thou hast heard me, and art become my salvation.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 O praise ye the Lord, for he is good: for his mercy endureth for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.