< Psalms 111 >

1 I will praise thee, O Lord, with my whole heart; in the council of the just: and in the congregation.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Great are the works of the Lord: sought out according to all his wills.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 His work is praise and magnificence: and his justice continueth for ever and ever.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 He hath made a remembrance of his wonderful works, being a merciful and gracious Lord:
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 He hath given food to them that fear him. He will be mindful for ever of his covenant:
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 He will shew forth to his people the power of his works.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 That he may give them the inheritance of the Gentiles: the works of his hands are truth and judgment.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 All his commandments are faithful: confirmed for ever and ever, made in truth and equity.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 He hath sent redemption to his people: he hath commanded his covenant for ever. Holy and terrible is his name:
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 The fear of the Lord is the beginning of wisdom. A good understanding to all that do it: his praise continueth for ever and ever.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalms 111 >