< Psalms 108 >

1 A canticle of a psalm for David himself. My heart is ready, O God, my heart is ready: I will sing, and will give praise, with my glory.
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Arise, my glory; arise, psaltery and harp: I will arise in the morning early.
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 I will praise thee, O Lord, among the people: and I will sing unto thee among the populations.
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 For thy mercy is great above the heavens: and thy truth even unto the clouds.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Be thou exalted, O God, above the heavens, and thy glory over all the earth:
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 That thy beloved may be delivered. Save with thy right hand and hear me.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 God hath spoken in his holiness. I will rejoice, and I will divide Sichem and I will mete out the vale of tabernacles.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 Galaad is mine, and Manasses is mine and Ephraim the protection of my head. Juda is my king:
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 Moab the pot of my hope. Over Edom I will stretch out my shoe: the aliens are become my friends.
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Who will bring me into the strong city? who will lead me into Edom?
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Wilt not thou, O God, who hast cast us off? and wilt not thou, O God, go forth with our armies?
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 O grant us help from trouble: for vain is the help of man.
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 Through God we shall do mightily: and he will bring our enemies to nothing.
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Psalms 108 >