< Proverbs 29 >

1 The man that with a stiff neck despiseth him that reproveth him, shall suddenly be destroyed: and health shall not follow him.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 When just men increase, the people shall rejoice: when the wicked shall bear rule, the people shall mourn.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 A man that loveth wisdom, rejoiceth his father: but he that maintaineth bar lots, shall squander away his substance.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 A just king setteth up the land: a covetous man shall destroy it.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 A man that speaketh to his friend with flattering and dissembling words, spreadeth a net for his feet.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 A snare shall entangle the wicked man when he sinneth: and the just shall praise and rejoice.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 The just taketh notice of the cause of the poor: the wicked is void of knowledge.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Corrupt men bring a city to ruin: but wise men turn away wrath.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 If a wise man contend with a fool, whether he be angry or laugh, he shall find no rest.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Bloodthirsty men hate the upright: but just men seek his soul.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 A fool uttereth all his mind: a wise man deferreth, and keepeth it till afterwards.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 A prince that gladly heareth lying words, hath all his servants wicked.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 The poor man and the creditor have met one another: the Lord is the enlightener of them both.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 The king that judgeth the poor in truth, his throne shall be established for ever.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 The rod and reproof give wisdom: but the child that is left to his own will bringeth his mother to shame.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 When the wicked are multiplied, crimes shall be multiplied: but the just shall see their downfall.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Instruct thy son, and he shall refresh thee, and shall give delight to thy soul.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 When prophecy shall fail, the people shall be scattered abroad: but he that keepeth the law is blessed.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 A slave will not be corrected by words: because he understandeth what thou sayest, and will not answer.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Hast thou seen a man hasty to speak? folly is rather to be looked for, than his amendment.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 He that nourisheth his servant delicately from his childhood, afterwards shall find him stubborn.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 A passionate man provoketh quarrels: and he that is easily stirred up to wrath, shall be more prone to sin.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Humiliation followeth the proud: and glory shall uphold the humble of spirit.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 He that is partaker with a thief, hateth his own soul: he heareth one putting him to his oath, and discovereth not.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 He that feareth man, shall quickly fall: he that trusteth in the Lord, shall be set on high.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Many seek the face of the prince: but the judgment of every one cometh forth from the Lord.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 The just abhor the wicked man: and the wicked loathe them that are in the right way. The son that keepeth the word, shall be free from destruction.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Proverbs 29 >