< Proverbs 2 >

1 My son, if thou wilt receive my words, and wilt hide my commandments with thee,
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 That thy ear may hearken to wisdom: Incline thy heart to know prudence:
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 For if thou shalt call for wisdom, and incline thy heart to prudence:
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 If thou shalt seek her as money, and shalt dig for her as for a treasure:
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Then shalt thou understand the fear of the Lord, and shalt find the knowledge of God.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Because the Lord giveth wisdom: and out of his mouth cometh prudence and knowledge.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 He will keep the salvation of the righteous, and protect them that walk in simplicity.
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 Keeping the paths of justice, and guarding the ways of saints.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Then shalt thou understand justice, and judgment, and equity, and every good path.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 If wisdom shall enter into thy heart, and knowledge please thy soul:
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Counsel shall keep thee, and prudence shall preserve thee,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 That thou mayst be delivered from the evil way, and from the man that speaketh perverse things:
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Who leave the right way, and walk by dark ways:
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Who are glad when they have done evil, and rejoice in most wicked things:
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Whose ways are perverse, and their steps infamous.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 That thou mayst be delivered from the strange women, and from the stranger, who softeneth her words:
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 And forsaketh the guide of her youth,
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 And hath forgotten the covenant of her God: for her house inclineth unto death, and her paths to hell. (questioned)
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 None that go in unto her shall return again, neither shall they take hold of the paths of life,
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 That thou mayst walk in a good way: and mayst keep the paths of the just.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 For they that are upright shall dwell in the earth, and the simple shall continue in it.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 But the wicked shall be destroyed from the earth: and they that do unjustly shall be taken away from it.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Proverbs 2 >