< Proverbs 16 >

1 It is the part of man to prepare the soul: and of the Lord to govern the tongue.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All the ways of a man are open to his eyes: the Lord is the weigher of spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Lay open thy works to the Lord: and thy thoughts shall be directed.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 The Lord hath made all things for himself: the wicked also for the evil day.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Every proud man is an abomination to the Lord: though hand should be joined to hand, he is not innocent. The beginning of a good way is to do justice; and this is more acceptable with God, than to offer sacrifices.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 By mercy and truth iniquity is redeemed: and by the fear of the Lord men depart from evil.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When the ways of man shall please the Lord, he will convert even his enemies to peace.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better is a little with justice, than great revenues with iniquity.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 The heart of man disposeth his way: but the Lord must direct his steps.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Divination is in the lips of the king, his mouth shall not err in judgment.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Weight and balance are judgments of the Lord: and his work all the weights of the bag.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 They that act wickedly are abominable to the king: for the throne is established by justice.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Just lips are the delight of kings: he that speaketh right things shall be loved.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 The wrath of a king is as messengers of death: and the wise man will pacify it.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the cheerfulness of the king’s countenance is life: and his clemency is like the latter rain.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Get wisdom, because it is better than gold: and purchase prudence, for it is more precious than silver.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 The path of the just departeth from evils: he that keepeth his soul keepeth his way.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pride goeth before destruction: and the spirit is lifted up before a fall.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 It is better to be humbled with the meek, than to divide spoils with the proud.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 The learned in word shall find good things: and he that trusteth in the Lord is blessed.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 The wise in heart shall be called prudent: and he that is sweet in words shall attain to greater things.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Knowledge is a fountain of life to him that possesseth it: the instruction of fools is foolishness.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of the wise shall instruct his mouth: and shall add grace to his lips.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Well ordered words are as a honeycomb: sweet to the soul, and health to the bones.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way that seemeth to a man right: and the ends thereof lead to death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 The soul of him that laboureth, laboureth for himself, because his mouth hath obliged him to it.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 The wicked man diggeth evil, and in his lips is a burning fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A perverse man stirreth up quarrels: and one full of words separateth princes.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 An unjust man allureth his friend: and leadeth him into a way that is not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 He that with fixed eyes deviseth wicked things, biting his lips, bringeth: evil to pass.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Old age is a crown of dignity, when it is found in the ways of justice.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 The patient man is better than the valiant: and he that ruleth his spirit than he that taketh cities.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Lots are cast into the lap, but they are disposed of by the Lord.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbs 16 >