< Numbers 31 >
1 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Revenge first the children of Israel on the Madianites, and so thou shalt be gathered to thy people.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 And Moses forthwith said: Arm of you men to fight, who may take the revenge of the Lord on the Madianites.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Let a thousand men be chosen out of every tribe of Israel to be sent to the war.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 And they gave a thousand of every tribe, that is to say, twelve thousand men well appointed for battle.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 And Moses sent them with Phinees the son of Eleazar the priest, and he delivered to him the holy vessels, and the trumpets to sound.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 And when they had fought against the Madianites and had overcome them, they slew all the men.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 And their kings Evi, and Recem, and Sur, and Hur, and Rebe, five princes of the nation: Balaam also the son of Beer they killed with the sword.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 And they took their women, and their children captives, and all their cattle, and all their goods: and all their possessions they plundered:
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 And all their cities, and their villages, and castles, they burned.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 And they carried away the booty, and all that they had taken both of men and of beasts.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 And they brought them to Moses, and Eleazar the priest, and to all the multitude of the children of Israel. But the rest of the things for use they carried to the camp on the plains of Moab, beside the Jordan over against Jericho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 And Moses and Eleazar the priest and all the princes of the synagogue went forth to meet them without the camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 And Moses being angry with the chief officers of the army, the tribunes, and the centurions that were come from the battle,
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Said: Why have you saved the women?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Are not these they, that deceived the children of Israel by the counsel of Balaam, and made you transgress against the Lord by the sin of Phogor, for which also the people was punished?
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Therefore kill all that are of the male sex, even of the children: and put to death the women, that have carnally known men.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 But the girls, and all the women that are virgins save for yourselves:
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 And stay without the camp seven days. He that hath killed a man, or touched one that is killed, shall be purified the third day and the seventh day.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 And of all the spoil, every garment, or vessel, or any thing made for use, of the skins, or hair of goats, or of wood, shall be purified.
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Eleazar also the priest spoke to the men of the army, that had fought, in this manner: This is the ordinance of the law, which the Lord hath commanded Moses:
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Gold, and silver, and brass, and iron, and lend, and tin,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 And all that may pass through the fire, shall be purified by fire, but whatsoever cannot abide the fire, shall be sanctified with the water of expiation:
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 And you shall wash your garments the seventh day, and being purified, you shall afterwards enter into the camp.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 And the Lord said to Moses:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Take the sum of the things that were taken both of man and beast, thou and Eleazar the priest and the princes of the multitude:
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 And thou shalt divide the spoil equally, between them that fought and went out to the war, and between the rest of the multitude.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 And thou shalt separate a portion to the Lord from them that fought and were in the battle, one soul of five hundred as well of persons as of oxen and asses and sheep.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 And thou shalt give it to Eleazar the priest, because they are the firstfruits of the Lord.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 Out of the moiety also of the children of Israel thou shalt take the fiftieth head of persons, and of oxen, and asses, and sheep, and of all beasts, and thou shalt give them to the Levites that watch in the charge of the tabernacle of the Lord.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 And Moses and Eleazar did as the Lord had commanded.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 And the spoil which the army had taken, was six hundred seventy-five thousand sheep,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 Seventy-two thousand oxen,
Ngʼombe 72,000,
34 Sixty-one thousand asses:
abulu 61,000,
35 And thirty-two thousand persons of the female sex, that had not known men.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 And one half was given to them that had been in the battle, to wit, three hundred thirty-seven thousand five hundred sheep:
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 Out of which, for the portion of the Lord, were reckoned six hundred seventy-five sheep.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 And out of the thirty-six thousand oxen, seventy-two oxen:
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Out of the thirty thousand five hundred asses, sixty-one asses:
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Out of the sixteen thousand persons, there fell to the portion of the Lord, thirty-two souls.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 And Moses delivered the number of the firstfruits of the Lord to Eleazar the priest, as had been commanded him,
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 Out of the half of the children of Israel, which he had separated for them that had been in the battle.
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 But out of the half that fell to the rest of the multitude, that is to say, out of the three hundred thirty-seven thousand five hundred sheep,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 And out of the thirty-six thousand oxen,
ngʼombe 36,000,
45 And out of the thirty thousand five hundred asses,
abulu 30,500,
46 And out of the sixteen thousand persons,
anthu 16,000.
47 Moses took the fiftieth head, and gave it to the Levites that watched in the tabernacle of the Lord, as the Lord had commanded.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 And when the commanders of the army, and the tribunes and centurions were come to Moses, they said:
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 We thy servants have reckoned up the number of the fighting men, whom we had under our hand, and not so much as one was wanting.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Therefore we offer as gifts to the Lord what gold every one of us could find in the booty, in garters and tablets, rings and bracelets, and chains, that thou mayst pray to the Lord for us.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 And Moses and Eleazar the priest received all the gold in divers kinds,
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 In weight sixteen thousand seven hundred and fifty sicles, from the tribunes and from the centurions.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 For that which every one had taken in the booty was his own.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 And that which was received they brought into the tabernacle of the testimony, for a memorial of the children of Israel before the Lord.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.