< Nehemiah 7 >
1 Now after the wall was built, and I had set up the doors, and numbered the porters and singing men, and Levites:
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 I commanded Hanani my brother, and Hananias ruler of the house of Jerusalem, (for he seemed as a sincere man, and one that feared God above the rest, )
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 And I said to them: Let not the gates of Jerusalem be opened till the sun be hot. And while they were yet standing by, the gates were shut, and barred: and I set watchmen of the inhabitants of Jerusalem, every one by their courses, and every mall over against his house.
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 And the city was very wide and great, and the people few in the midst thereof, and the houses were not built.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 But God had put in my heart, and I assembled the princes and magistrates, and common people, to number them: and I found a book of the number of them who came up at first, and therein it was found written:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 These are the children of the province, who came up from the captivity of them that had been carried away, whom Nabuchodonosor the king of Babylon had carried away, and who returned into Judea, every one into his own city.
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 Who came with Zorobabel, Josue, Nehemias, Azarias, Raamias, Nahamani, Mardochai, Belsam, Mespharath, Begoia, Nahum, Baana. The number of the men of the people of Israel:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 The children of Pharos, two thousand one hundred seventy-two.
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 The children of Sephatia, three hundred seventy-two.
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 The children of Area, six hundred fifty-two.
Zidzukulu za Ara 652
11 The children of Phahath Moab of the children of Josue and Joab, two thousand eight hundred eighteen.
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 The children of Elam, one thousand two hundred fifty-four.
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 The children of Zethua, eight hundred forty-five.
Zidzukulu za Zatu 845
14 The children of Zachai, seven hundred sixty.
Zidzukulu za Zakai 760
15 The children of Bannui, six hundred forty-eight.
Zidzukulu za Binuyi 648
16 The children of Bebai, six hundred twenty-eight.
Zidzukulu za Bebai 628
17 The children of Azgad, two thousand three hundred twenty-two.
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 The children of Adonicam, six hundred sixty-seven.
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 The children of Beguai, two thousand sixty-seven.
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 The children of Adin, six hundred fifty-five.
Zidzukulu za Adini 655
21 The children of Ater, children of Hezechias, ninety-eight.
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 The children of Hasem, three hundred twenty-eight.
Zidzukulu za Hasumu 328
23 The children of Besai, three hundred twenty-four.
Zidzukulu za Bezayi 324
24 The children of Hareph, a hundred and twelve.
Zidzukulu za Harifu 112
25 The children of Gabaon, ninety-five.
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 The children of Bethlehem, and Netupha, a hundred eighty-eight.
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 The men of Anathoth, a hundred twenty-eight.
Anthu a ku Anatoti 128
28 The men of Bethazmoth, forty-two.
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 The men of Cariathiarim, Cephira, and Beroth, seven hundred forty-three.
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 The men of Rama and Geba, six hundred twenty-one.
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 The men of Machmas, a hundred twenty-two.
Anthu a ku Mikimasi 122
32 The men of Bethel and Hai, a hundred twenty-three.
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 The men of the other Nebo, fifty-two.
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 The men of the other Elam, one thousand two hundred fifty-four.
Ana a Elamu wina 1,254
35 The children of Harem, three hundred and twenty.
Zidzukulu za Harimu 320
36 The children of Jericho, three hundred forty-five.
Zidzukulu za Yeriko 345
37 The children of Led, of Hadid and One, seven hundred twenty-one.
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 The children of Senaa, three thousand nine hundred thirty.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 The priests: the children of Idaia in the house of Josue, nine hundred and seventy-three.
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 The children of Emmer, one thousand fifty-two.
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 The children of Phashur, one thousand two hundred forty-seven.
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 The children of Arem, one thousand and seventeen. The Levites:
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 The children of Josue and Cedmihel, the sons
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Of Oduia, seventy-four. The singing men:
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 The children of Asaph, a hundred forty-eight.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 The porters: the children of Sellum, the children of Ater, the children of Telmon, the children of Accub, the children of Hatita, the children of Sobai: a hundred thirty-eight.
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 The Nathinites: the children of Soha, the children of Hasupha, the children of Tebbaoth,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 The children of Ceros, the children of Siaa, the children of Phadon, the children of Lebana, the children of Hagaba, the children of Selmai,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 The children of Hanan, the children of Geddel, the children of Gaher,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 The children of Raaia, the children of Rasin, the children of Necoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 The children of Gezem, the children of Asa, the children of Phasea,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 The children of Besai, the children of Munim, the children of Nephussim,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 The children of Bacbuc, the children of Hacupha, the children of Harhur,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 The children of Besloth, the children of Mahida, the children of Harsa,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 The children of Bercos, the children of Sisara, the children of Thema,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 The children of Nasia, the children of Hatipha,
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 The children of the servants of Solomon, the children of Sothai, the children of Sophereth, the children of Pharida,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 The children of Jahala, the children of Darcon, the children of Jeddel,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 The children of Saphatia, the children of Hatil, the children of Phochereth, who was born of Sabaim, the son of Amon.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 All the Nathinites, and the children of the servants of Solomon, three hundred ninety-two.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 And these are they that came up from Telmela, Thelharsa, Cherub, Addon, and Emmer: and could not shew the house of their fathers, nor their seed, whether they were of Israel.
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 The children of Dalaia, the children of Tobia, the children of Necoda, six hundred forty-two.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 And of the priests, the children of Habia, the children of Accos, the children of Berzellai, who took a wife of the daughters of Berzellai the Galaadite, and he was called by their name.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 These sought their writing in the record, and found it not: and they were cast out of the priesthood.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 And Athersatha said to them, that they should not eat of the holies of holies, until there stood up a priest learned and skillful.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 All the multitude as it were one man, forty-two thousand three hundred sixty,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 Beside their menservants and womenservants, who were seven thousand three hundred thirty-seven: and among them singing men, and singing women, two hundred forty-five.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Their horses, seven hundred thirty-six: their mules two hundred forty-five:
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 Their camels, four hundred thirty-five, their asses, six thousand seven hundred and twenty.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 And some of the heads of the families gave unto the work. Athersatha gave into the treasure a thousand drama of gold, fifty bowls, and five hundred and thirty garments for priests.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 And some of the heads of families gave to the treasure of the work, twenty thousand drama of gold, and two thousand two hundred pounds of silver.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 And that which the rest of the people gave, was twenty thousand drama of gold, and two thousand pounds of silver, and sixty-seven garments for priests.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 And the priests, and the Levites, and the porters, and the singing men, and the rest of the common people, and the Nathinites, and all Israel dwelt in their cities.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.