< Nehemiah 13 >

1 And on that day they read in the book of Moses in the hearing of the people: and therein was found written, that the Ammonites and the Moabites should not come in to the church of God for ever:
Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
2 Because they met not the children of Israel with bread and water: and they hired against them Balaam, to curse them, and our God turned the curse into blessing.
Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
3 And it came to pass, when they had heard the law, that they separated every stranger from Israel.
Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
4 And over this thing was Eliasib the priest, who was set over the treasury of the house of our God, and was near akin to Tobias.
Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
5 And he made him a great storeroom, where before him they laid up gifts, and frankincense, and vessels, and the tithes of the corn, of the wine, and of the oil, the portions of the Levites, and of the singing men, and of the porters, and the firstfruits of the priests.
Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
6 But in all this time I was not in Jerusalem, because in the two and thirtieth year of Artaxerxes king of Babylon, I went to the king, and after certain days I asked the king:
Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
7 And I came to Jerusalem, and I understood the evil that Eliasib had done for Tobias, to make him a storehouse in the courts of the house of God.
ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
8 And it seemed to me exceeding evil. And I cast forth the vessels of the house of Tobias out of the storehouse.
Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
9 And I commanded and they cleansed the storehouses: and I brought thither again the vessels of the house of God, the sacrifice, and the frankincense.
Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
10 And I perceived that the portions of the Levites had not been given them: and that the Levites, and the singing men, and they that ministered were fled away every man to his own country:
Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
11 And I pleaded the matter against the magistrates, and said: Why have we forsaken the house of God? And I gathered them together, and I made them to stand in their places.
Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
12 And all Juda brought the tithe of the corn, and the wine, and the oil into the storehouses.
Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
13 And we set over the storehouses Selemias the priest, and Sadoc the scribe, and of the Levites Phadaia, and next to them Hanan the son of Zachur, the son of Mathania: for they were approved as faithful, and to them were committed the portions of their brethren.
Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
14 Remember me, O my God, for this thing, and wipe not out my kindnesses, which I have done relating to the house of my God and his ceremonies.
Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
15 In those days I saw in Juda some treading the presses on the sabbath, and carrying sheaves, and lading asses with wine, and grapes, and figs, and all manner of burthens, and bringing them into Jerusalem on the sabbath day. And I charged them that they should sell on a day on which it was lawful to sell.
Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
16 Some Tyrians also dwelt there, who brought fish, and all manner of wares: and they sold them on the sabbaths to the children of Juda in Jerusalem.
Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
17 And I rebuked the chief men of Juda, and said to them: What is this evil thing that you are doing, profaning the sabbath day?
Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
18 Did not our fathers do these things, and our God brought all this evil upon us, and upon this city? And you bring more wrath upon Israel by violating the sabbath.
Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
19 And it came to pass, that when the gates of Jerusalem were at rest on the sabbath day, I spoke: and they shut the gates, and I commanded that they should not open them till after the sabbath: and I set some of my servants at the gates, that none should bring in burthens on the sabbath day.
Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
20 So the merchants, and they that sold all kinds of wares, stayed without Jerusalem once or twice.
Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
21 And I charged them, and I said to them: Why stay you before the wall? if you do so another time, I will lay hands on you. And from that time they came no more on the sabbath.
Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
22 I spoke also to the Levites that they should be purified, and should come to keep the gates, and to sanctify the sabbath day: for this also remember me, O my God, and spare me according to the multitude of thy tender mercies.
Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
23 In those days also I saw Jews that married wives, women of Azotus, and of Ammon, and of Moab.
Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
24 And their children spoke half in the speech of Azotus, and could not speak the Jews’ language, but they spoke according to the language of this and that people.
Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
25 And I chid them, and laid my curse upon them. And I beat some of them, and shaved off their hair, and made them swear by God that they would not give their daughters to their sons, nor take their daughters for their sons, nor for themselves, saying:
Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
26 Did not Solomon king of Israel sin in this kind of thing? and surely among many nations, there was not a king like him, and he was beloved of his God, and God made him king over all Israel: and yet women of other countries brought even him to sin.
Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
27 And shall we also be disobedient and do all this great evil to transgress against our God, and marry strange women?
Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
28 And one of the sons of Joiada the son of Eliasib the high priest, was son in law to Sanaballat the Horonite, and I drove him from me.
Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
29 Remember them, O Lord my God, that defile the priesthood, and the law of priests and Levites.
Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
30 So I separated from them all strangers, and I appointed the courses of the priests and the Levites, every man in his ministry:
Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
31 And for the offering of wood at times appointed, and for the firstfruits: remember me, O my God, unto good. Amen.
Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.

< Nehemiah 13 >