< Nehemiah 11 >
1 And the princes of the people dwelt at Jerusalem: but the rest of the people cast lots, to take one part in ten to dwell in Jerusalem the holy city, and nine parts in the other cities.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 And the people blessed all the men that willingly offered themselves to dwell in Jerusalem.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 These therefore are the chief men of the province, who dwelt in Jerusalem, and in the cities of Juda. And every one dwelt in his possession, in their cities: Israel, the priests, the Levites, the Nathinites, and the children of the servants of Solomon.
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 And in Jerusalem there dwelt some of the children of Juda, and some of the children of Benjamin: of the children of Juda, Athaias the son of Aziam, the son of Zacharias, the son of Amarias, the son of Saphatias, the son of Malaleel: of the sons of Phares,
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 Maasia the son of Baruch, the son of Cholhoza, the son of Hazia, the son of Adaia, the son of Joiarib, the son of Zacharias, the son of the Silonite:
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 All these the sons of Phares, who dwelt in Jerusalem, were four hundred sixty-eight valiant men.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 And these are the children of Benjamin: Sellum the son of Mosollam, the son of Joed, the son of Phadaia, the son of Colaia, the son of Masia, the son of Etheel, the son of Isaia.
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 And after him Gebbai, Sellai, nine hundred twenty-eight.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 And Joel the son of Zechri their ruler, and Judas the son of Senua was second over the city.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 And of the priests Idaia the son of Joarib, Jachin,
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Saraia the son of Helcias, the son of Mosollam, the son of Sadoc, the son of Meraioth, the son of Achitob the prince of the house of God,
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 And their brethren that do the works of the temple: eight hundred twenty-two. And Adaia the son of Jeroham, the son of Phelelia, the son of Amsi, the son of Zacharias, the son of Pheshur, the son of Melchias,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 And his brethren the chiefs of the fathers: two hundred forty-two. And Amassai the son of Azreel, the son of Ahazi, the son of Mosollamoth, the son of Emmer,
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 And their brethren who were very mighty, a hundred twenty-eight: and their ruler Zabdiel son of the mighty.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 And of the Levites Semeia the son of Hasub, the son of Azaricam, the son of Hasabia, the son of Boni,
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 And Sabathai and Jozabed, who were over all the outward business of the house of God, of the princes of the Levites,
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 And Mathania the son of Micha, the son of Zebedei, the son of Asaph, was the principal man to praise, and to give glory in prayer, and Becbecia the second, one of his brethren, and Abda the son of Samua, the son of Galal, the son of Idithun.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 All the Levites in the holy city were two hundred eighty-four.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 And the porters, Accub, Telmon, and their brethren, who kept the doors: a hundred seventy-two.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 And the rest of Israel, the priests and the Levites were in all the cities of Juda, every man in his possession.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 And the Nathinites, that dwelt in Ophel, and Siaha, and Gaspha of the Nathinites.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 And the overseer of the Levites in Jerusalem, was Azzi the son of Bani, the son of Hasabia, the son of Mathania, the son of Micha. Of the sons of Asaph, were the singing men in the ministry of the house of God.
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 For the king’s commandment was concerning them, and an order among the singing men day by day.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 And Phathahia the son of Mesezebel of the children of Zara the son of Juda was at the hand of the king, in all matters concerning the people,
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 And in the houses through all their countries. Of the children of Juda so dwelt at Cariath-Arbe, and in the villages thereof: and at Dibon, and in the villages thereof: and at Cabseel, and in the villages thereof.
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 And at Jesue, and at Molada, and Bethphaleth,
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 And at Hasersual, and at Bersabee, and in the villages thereof,
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 And at Siceleg, and at Mochona, and in the villages thereof,
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 And at Remmon, and at Saraa, and at Jerimuth,
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 Zanoa, Odollam, and in their villages, at Lachis and its dependencies, and at Azeca and the villages thereof. And they dwelt from Bersabee unto the valley of Ennom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 And the children of Benjamin, from Geba, at Mechmas, and at Hai, and at Bethel, and in the villages thereof,
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 At Anathoth, Nob, Anania,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 Hadid, Seboim, and Neballat, Led,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 And Ono the valley of craftsmen.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 And of the Levites were portions of Juda and Benjamin.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.