< Lamentations 3 >

1 Aleph. I am the man that see my poverty by the rod of his indignation.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Aleph. He hath led me, and brought me into darkness, and not into light.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Aleph. Only against me he hath turned, and turned again his hand all the day.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Beth. My skin and my flesh he hath made old, he hath broken my bones.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Beth. He hath built round about me, and he hath compassed me with gall and labour.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Beth. He hath set me in dark places as those that are dead for ever.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Ghimel. He hath built against me round about, that I may not get out: he hath made my fetters heavy.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Ghimel. Yea, and when I cry, and entreat, he hath shut out my prayer.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Ghimel. He hath shut up my ways with square stones, he hath turned my paths upside down.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Daleth. He is become to me as a bear lying in wait: as a lion in secret places.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Daleth. He hath turned aside my paths, and hath broken me in pieces, he hath made me desolate.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Daleth. He hath bent his bow, and set me as a mark for his arrows.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He. He hath shot into my reins the daughters of his quiver.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 He. I am made a derision to all my people, their song all the day long.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He. He hath filled me with bitterness, he hath inebriated me with wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Vau. And he hath broken my teeth one by one, he hath fed me with ashes.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Vau. And my soul is removed far off from peace, I have forgotten good things.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Vau. And I said: My end and my hope is perished from the Lord.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Zain. Remember my poverty, and transgression, the wormwood, and the gall.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Zain. I will be mindful and remember, and my soul shall languish within me.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Zain. These things I shall think over in my heart, therefore will I hope.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Heth. The mercies of the Lord that we are not consumed: because his commiserations have not failed.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Heth. They are new every morning, great is thy faithfulness.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Heth. The Lord is my portion, said my soul: therefore will I wait for him.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Teth. The Lord is good to them that hope in him, to the soul that seeketh him.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Teth. It is good to wait with silence for the salvation of God.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Teth. It is good for a man, when he hath borne the yoke from his youth.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Jod. He shall sit solitary, and hold his peace: because he hath taken it up upon himself.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Jod. He shall put his mouth in the dust, if so be there may be hope.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Jod. He shall give his cheek to him that striketh him, he shall be filled with reproaches.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Caph. For the Lord will not cast off for ever.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Caph. For if he hath cast off, he will also have mercy, according to the multitude of his mercies.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Caph. For he hath not willingly afflicted, nor cast off the children of men.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Lamed. To crush under his feet all the prisoners of the land,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Lamed. To turn aside the judgment of a man before the face of the most High,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Lamed. To destroy a man wrongfully in his judgment, the Lord hath not approved.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Mem. Who is he that hath commanded a thing to be done, when the Lord commandeth it not?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Mem. Shall not both evil and good proceed out of the mouth of the Highest?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Mem. Why hath a living man murmured, man suffering for his sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Nun. Let us search our ways, and seek, and return to the Lord.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Nun. Let us lift up our hearts with our hands to the Lord in the heavens.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 Nun. We have done wickedly, and provoked thee to wrath: therefore thou art inexorable.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Samech. Thou hast covered in thy wrath, and hast struck us: thou hast killed and hast not spared.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Samech. Thou hast set a cloud before thee, that our prayer may not pass through.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Samech. Thou hast made me as an outcast, and refuse in the midst of the people.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 Phe. All our enemies have opened their mouths against us.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Phe. Prophecy is become to us a fear, and a snare, and destruction.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Phe. My eye hath run down with streams of water, for the destruction of the daughter of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Ain. My eye is afflicted, and hath not been quiet, because there was no rest:
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Ain. Till the Lord regarded and looked down from the heavens.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Ain. My eye hath wasted my soul because of all the daughters of my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Sade. My enemies have chased me and caught me like a bird, without cause.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Sade. My life is fallen into the pit, and they have laid a stone over me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Sade. Waters have flowed over my head: I said: I am cut off.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Coph. I have called upon thy name, O Lord, from the lowest pit.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Coph. Thou hast heard my voice: turn not away thy ear from my sighs, and cries.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Coph. Thou drewest near in the day, when I called upon thee, thou saidst: Fear not.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Res. Thou hast judged, O Lord, the cause of my soul, thou the Redeemer of my life.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Res. Thou hast seen, O Lord, their iniquity against me: judge thou my judgment.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Res. Thou hast seen all their fury, and all their thoughts against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Sin. Thou hast heard their reproach, O Lord, all their imaginations against me.
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 Sin. The lips of them that rise up against me: and their devices against me all the day.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Sin. Behold their sitting down, and their rising up, I am their song.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Thau. Thou shalt render them a recompense, O Lord, according to the works of their hands.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Thau. Thou shalt give them a buckler of heart, thy labour.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Thau. Thou shalt persecute them in anger, and shalt destroy them from under the heavens, O Lord.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >