< Joshua 6 >
1 Now Jericho was close shut up and fenced, for fear of the children of Israel, and no man durst go out or come in.
Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
2 And the Lord said to Josue: Behold I have given into thy hands Jericho, and the king thereof, and all the valiant men.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
3 Go round about the city, all ye fighting men, once a day: so shall ye do for six days.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
4 And on the seventh day the priests shall take the seven trumpets, which are used in the jubilee, and shall go before the ark of the covenant: and you shall go about the city seven times, and the priests shall sound the trumpets.
Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
5 And when the voice of the trumpet shall give a longer and broken tune, and shall sound in your ears, all the people shall shout together with a very great shout, and the walls of the city shall fall to the ground, and they shall enter in every one at the place against which they shall stand.
Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
6 Then Josue the son of Nun called the priests, and said to them: Take the ark of the covenant: and let seven other priests take the seven trumpets of the jubilee, and march before the ark of the Lord.
Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
7 And he said to the people: Go, and compass the city, armed, marching before the ark of the Lord.
Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
8 And when Josue had ended his words, and the seven priests blew the seven trumpets before the ark of the covenant of the Lord,
Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
9 And all the armed men went before, the rest of the common people followed the ark, and the sound of the trumpets was heard on all sides.
Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
10 But Josue had commanded the people, saying: You shall not shout, nor shall your voice be heard, nor any word go out of your mouth: until the day come wherein I shall say to you: Cry, and shout.
Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
11 So the ark of the Lord went about the city once a day, and returning into the camp, abode there.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
12 And Josue rising before day, the priests took the ark of the Lord,
Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
13 And seven of them seven trumpets, which are used in the jubilee: and they went before the ark of the Lord walking and sounding the trumpets: and the armed men went before them, and the rest of the common people followed the ark, and they blew the trumpets.
Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
14 And they went round about the city the second day once, and returned into the camp. So they did six days.
Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
15 But the seventh day, rising up early, they went about the city, as it was ordered, seven times.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
16 And when in the seventh going about the priests sounded with the trumpets, Josue said to all Israel: Shout: for the Lord hath delivered the city to you:
Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
17 And let this city be an anathema, and all things that are in it, to the Lord. Let only Rahab the harlot live, with all that are with her in the house: for she hid the messengers whom we sent.
Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
18 But beware ye lest you touch ought of those things that are forbidden, and you be guilty of transgression, and all the camp of Israel be under sin, and be troubled.
Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
19 But whatsoever gold or silver there shall be, or vessels of brass and iron, let it be consecrated to the Lord, laid up in his treasures.
Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
20 So all the people making a shout, and the trumpets sounding, when the voice and the sound thundered in the ears of the multitude, the walls forthwith fell down: and every man went up by the place that was over against him: and they took the city,
Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
21 And killed all that were in it, man and woman, young and old. The oxen also and the sheep, and the asses, they slew with the edge of the sword.
Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
22 But Josue said to the two men that had been sent for spies: Go into the harlot’s house, and bring her out, and all things that are hers, as you assured her by oath.
Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
23 And the young men went in and brought out Rahab, and her parents, her brethren also and all her goods and her kindred, and made them to stay without the camp.
Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
24 But they burned the city, and all things that were therein; except the gold and silver, and vessels of brass and iron, which they consecrated into the treasury of the Lord.
Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
25 But Josue saved Rahab the harlot and her father’s house, and all she had, and they dwelt in the midst of Israel until this present day: because she hid the messengers whom he had sent to spy out Jericho. At that time, Josue made an imprecation, saying:
Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
26 Cursed be the man before the Lord, that shall raise up and build the city of Jericho. In his firstborn may he lay the foundation thereof, and in the last of his children set up its gates.
Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
27 And the Lord was with Josue, and his name was noised throughout all the land.
Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.