< Joshua 19 >

1 And the second lot came forth for the children of Simeon by their kindreds: and their inheritance was
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 In the midst of the possession of the children of Juda: Bersabee and Sabee and Molada,
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 And Hasersual, Bala and Asem,
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 And Eltholad, Bethul and Harma,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 And Siceleg and Bethmarchaboth and Hasersusa,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 And Bethlebaoth and Sarohen: thirteen cities, and their villages.
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Ain and Remmon and Athor and Asan: four cities, and their villages.
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 And all the villages round about these cities to Baalath Beer Ramath to the south quarter. This is the inheritance of the children of Simeon according to their kindreds,
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 In the possession and lot of the children of Juda: because it was too great, and therefore the children of Simeon had their possession in the midst of their inheritance.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 And the third lot fell to the children of Zabulon by their kindreds: and the border of their possession was unto Sarid.
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 And it went up from the sea and from Merala, and came to Debbaseth: as far as the torrent, which is over against Jeconam.
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 And it returneth from Sarid eastward to the borders of Ceseleththabor: and it goeth out to Dabereth, and ascendeth towards Japhie.
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 And it passeth along from thence to the east side of Gethhepher and Thacasin: and goeth out to Remmon, Amthar and Noa.
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 And it turneth about to the north of Hanathon: and the outgoings thereof are the valley of Jephtahel,
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 And Cateth and Naalol and Semeron and Jedala and Bethlehem: twelve cities and their villages.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 This is the inheritance of the tribe of the children of Zabulon by their kindreds, the cities and their villages.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 The fourth lot came out to Issachar by their kindreds.
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 And his inheritance was Jezrael and Casaloth and Sunem,
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 And Hapharaim and Seen and Anaharath,
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 And Rabboth and Cesion, Abes,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 And Rameth and Engannim and Enhadda and Bethpheses.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 And the border thereof cometh to Thabor and Sehesima and Bethsames: and the outgoings thereof shall be at the Jordan: sixteen cities, and their villages.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 This is the possession of the sons of Issachar by their kindreds, the cities and their villages.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 And the fifth lot fell to the tribe of the children of Aser by their kindreds:
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 And their border was Halcath and Chali and Beten and Axaph,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 And Elmelech and Amaad and Messal: and it reacheth to Carmel by the sea and Sihor and Labanath,
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 And it returneth towards the east to Bethdagon: and passeth along to Zabulon and to the valley of Jephthael towards the north to Bethemec and Nehiel. And it goeth out to the left side of Cabul,
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 And to Abaran and Rohob and Hamon and Cana, as far as the great Sidon.
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 And it returneth to Horma to the strong city of Tyre, and to Hosa: and the outgoings thereof shall be at the sea from the portion of Achziba:
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 And Amma and Aphec and Rohob: twenty-two cities, and their villages.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 This is the possession of the children of Aser by their kindreds, and the cities and their villages.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 The sixth lot came out to the sons of Nephtali by their families:
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 And the border began from Heleph and Elon to Saananim, and Adami, which is Neceb, and Jebnael even to Lecum: and their outgoings unto the Jordan:
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 And the border returneth westward to Azanotthabor, and goeth out from thence to Hucuca, and passeth along to Zabulon southward, and to Aser westward, and to Juda upon the Jordan towards the rising of the sun.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 And the strong cities are Assedim, Ser, and Emath, and Reccath and Cenereth,
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 And Edema and Arama, Asor,
Adama, Rama, Hazori,
37 And Cedes and Edri, Enhasor,
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 And Jeron and Magdalel, Herem, and Bethanath and Bethsames: nineteen cities, and their villages.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 This is the possession of the tribe of the children of Nephtali by their kindreds, the cities and their villages.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 The seventh lot came out to the tribe of the children of Dan by their families:
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 And the border of their possession was Saraa and Esthaol, and Hirsemes, that is, the city of the sun.
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Selebin and Aialon and Jethela,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Elon and Themna and Acron,
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Elthece, Gebbethon and Balaath,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 And Jud and Bane and Barach and Gethremmon:
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 And Mejarcon and Arecon, with the border that looketh towards Joppe,
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 And is terminated there. And the children of Dan went up and fought against Lesem, and took it: and they put it to the sword, and possessed it, and dwelt in it, calling the name of it Lesem Dan, by the name of Dan their father.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 This is the possession of the tribe of the sons of Dan, by their kindreds, the cities and their villages.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 And when he had made an end of dividing the land by lot to each one by their tribes, the children of Israel gave a possession to Josue the son of Nun in the midst of them,
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 According to the commandment of the Lord, the city which he asked for, Thamnath Saraa, in mount Ephraim: and he built up the city, and dwelt in it.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 These are the possessions which Eleazar the priest, and Josue the son of Nun, and the princes of the families, and of the tribes of the children of Israel, distributed by lot in Silo, before the Lord at the door of the tabernacle of the testimony, and they divided the land.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Joshua 19 >