< Job 4 >
1 Then Eliphaz the Themanite answered, and said:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 If we begin to speak to thee, perhaps thou wilt take it ill, but who can withhold the words he hath conceived?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Behold thou hast taught many, and thou hast strengthened the weary hands:
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Thy words have confirmed them that were staggering, and thou hast strengthened the trembling knees:
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 But now the scourge is come upon thee, and thou faintest: it hath touched thee, and thou art troubled.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Where is thy fear, thy fortitude, thy patience, and the perfection of thy ways?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 Remember, I pray thee, who ever perished being innocent? or when were the just destroyed?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 On the contrary I have seen those who work iniquity, and sow sorrows, and reap them,
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 Perishing by the blast of God, and consumed by the spirit of his wrath.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 The roaring of the lion, and the voice of the lioness, and the teeth of the whelps of lions are broken:
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 The tiger hath perished for want of prey, and the young lions are scattered abroad.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 Now there was a word spoken to me in private, and my ears by stealth as it were received the veins of its whisper.
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 In the horror of a vision by night, when deep sleep is wont to hold men,
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 Fear seized upon me, and trembling, and all my bones were affrighted:
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 And when a spirit passed before me, the hair of my flesh stood up.
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 There stood one whose countenance I knew not, an image before my eyes, and I heard the voice as it were of a gentle wind:
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 Shall man be justified in comparison of God, or shall a man be more pure than his maker?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Behold they that serve him are not steadfast, and in his angels he found wickedness:
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 How much more shall they that dwell in houses of clay, who have an earthly foundation, be consumed as with the moth?
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 From morning till evening they shall be cut down: and because no one understandeth, they shall perish for ever.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 And they that shall be left, shall be taken away from them: they shall die, and not in wisdom.
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’