< Job 38 >

1 Then the Lord answered Job out of a whirlwind, and said:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 Who is this that wrappeth up sentences in unskillful words?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Gird up thy loins like a man: I will ask thee, and answer thou me.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Where wast thou when I laid up the foundations of the earth? tell me if thou hast understanding.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Who hath laid the measures thereof, if thou knowest? or who hath stretched the line upon it?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Upon what are its bases grounded? or who laid the corner stone thereof,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 When the morning stars praised me together, and all the sons of God made a joyful melody?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Who shut up the sea with doors, when it broke forth as issuing out of the womb:
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 When I made a cloud the garment thereof, and wrapped it in a mist as in swaddling bands?
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 I set my bounds around it, and made it bars and doors:
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 And I said: Hitherto thou shalt come, and shalt go no further, and here thou shalt break thy swelling waves.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Didst thou since thy birth command the morning, and shew the dawning of the day its place?
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 And didst thou hold the extremities of the earth shaking them, and hast thou shaken the ungodly out of it?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 The seal shall be restored as clay, and shall stand as a garment:
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 From the wicked their light shall be taken away, and the high arm shall be broken.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Hast thou entered into the depths of the sea, and walked in the lowest parts of the deep?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Have the gates of death been opened to thee, and hast thou seen the darksome doors?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Hast thou considered the breadth of the earth? tell me, if thou knowest all things?
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Where is the way where light dwelleth, and where is the place of darkness:
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 That thou mayst bring every thing to its own bounds, and understand the paths of the house thereof.
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Didst thou know then that thou shouldst be born? and didst thou know the number of thy days?
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Hast thou entered into the storehouses of the snow, or has thou beheld the treasures of the hail:
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Which I have prepared for the time of the enemy, against the day of battle and war?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 By what way is the light spread, and heat divided upon the earth?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Who gave a course to violent showers, or a way for noisy thunder:
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 That it should rain on the earth without man in the wilderness, where no mortal dwelleth:
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 That it should fill the desert and desolate land, and should bring forth green grass?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Who is the father of rain? or who begot the drops of dew?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Out of whose womb came the ice; and the frost from heaven who hath gendered it?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 The waters are hardened like a stone, and the surface of the deep is congealed.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Shalt thou be able to join together the shining stars the Pleiades, or canst thou stop the turning about of Arcturus?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Canst thou bring forth the day star in its time, and make the evening star to rise upon the children of the earth?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Dost thou know the order of heaven, and canst thou set down the reason thereof on the earth?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Canst thou lift up thy voice to the clouds, that an abundance of waters may cover thee?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Canst thou send lightnings, and will they go, and will they return and say to thee: Here we are?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Who hath put wisdom in the heart of man? or who gave the cock understanding?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Who can declare the order of the heavens, or who can make the harmony of heaven to sleep?
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 When was the dust poured on the earth, and the clods fastened together?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Wilt thou take the prey for the lioness, and satisfy the appetite of her whelps,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 When they couch in the dens and lie in wait in holes?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Who provideth food for the raven, when her young ones cry to God, wandering about, because they have no meat?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >