< Job 29 >

1 Job also added, taking up his parable, and said:
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Who will grant me, that I might be according to the months past, according to the days in which God kept me?
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 When his lamp shined over my head, and I walked by his light in darkness?
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 As I was in the days of my youth, when God was secretly in my tabernacle?
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 When the Almighty was with me: and my servants round about me?
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 When I washed my feet with butter, and the rock poured me out rivers of oil?
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 When I went out to the gate of the city, and in the street they prepared me a chair?
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 The young men saw me, and hid themselves: and the old men rose up and stood.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 The princes ceased to speak, and laid the finger on their mouth.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 The rulers held their peace, and their tongue cleaved to their throat.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 The ear that heard me blessed me, and the eye that saw me gave witness to me:
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 Because I had delivered the poor man that cried out; and the fatherless that had no helper.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 The blessing of him that was ready to perish came upon me, and I comforted the heart of the widow.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 I was clad with justice: and I clothed myself with my judgment, as with a robe and a diadem.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 I was an eye to the blind, and a foot to the lame.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 I was the father of the poor: and the cause which I knew not, I searched out most diligently.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 I broke the jaws of the wicked man, and out of his teeth I took away the prey.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 And I said: I shall die in my nest, and as a palm tree shall multiply my days.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 My root is opened beside the waters, and dew shall continue in my harvest.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 My glory shall always be renewed, and my bow in my hand shall be repaired.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 They that heard me, waited for my sentence, and being attentive held their peace at my counsel.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 To my words they durst add nothing, and my speech dropped upon them.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 They waited for me as for rain, and they opened their mouth as for a latter shower.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 If at any time I laughed on them, they believed not, and the light of my countenance fell not on earth.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 If I had a mind to go to them, I sat first, and when I sat as a king, with his army standing about him, yet I was a comforter of them that mourned.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >