< Job 20 >

1 Then Sophar the Naamathite answered, and said:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Therefore various thoughts succeed one another in me, and my mind is hurried away to different things.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 The doctrine with which thou reprovest me, I will hear, and the spirit of my understanding shall answer for me.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 This I know from the beginning, since man was placed upon the earth,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 That the praise of the wicked is short, and the joy of the hypocrite but for a moment.
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 If his pride mount up even to heaven, and his head touch the clouds:
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 In the end he shall be destroyed like a dunghill, and they that has seen him shall say: Where is he?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 As a dream that fleeth away he shall not be found, he shall pass as a vision of the night:
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 The eyes that had seen him, shall see him no more, neither shall his place any more behold him.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 His children shall be oppressed with want, and his hands shall render him his sorrow.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 His bones shall be filled with the vices of his youth, and they shall sleep with him in the dust.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 For when evil shall be sweet in his mouth, he will hide it under his tongue.
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 He will spare it, and not leave it, and will hide it in his throat.
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 His bread in his belly shall be turned into the gall of asps within him.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 The riches which he hath swallowed; he shall vomit up, and God shall draw them out of his belly.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 He shall suck the head of asps, and the viper’s tongue shall kill him.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 (Let him not see the streams of the river, the brooks of honey and of butter.)
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 He shall be punished for all that he did, and yet shall not be consumed: according to the multitude of his devices so also shall he suffer.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Because he broke in and stripped the poor: he hath violently taken away a house which he did not build.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 And yet his belly was not filled: and when he hath the things he coveted, he shall not be able to possess them.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 There was nothing left of his meat, and therefore nothing shall continue of his goods:
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 When he shall be filled, he shall be straitened, he shall burn, and every sorrow shall fall upon him.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 May his belly be filled, that God may send forth the wrath of his indignation upon him, and rain down his war upon him.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 He shall flee from weapons of iron, and shall fall upon a bow of brass.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 The sword is drawn out, and cometh forth from its scabbard, and glittereth in his bitterness: the terrible ones shall go and come upon him.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 All darkness is hid in his secret places: a fire that is not kindled shall devour him, he shall be afflicted when left in his tabernacle.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 The heavens shall reveal his iniquity, and the earth shall rise up against him.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 The offspring of his house shall be exposed, he shall be pulled down in the day of God’s wrath.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 This is the portion of a wicked man from God, and the inheritance of his doings from the Lord.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >