< Job 16 >

1 Then Job answered, and said:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 I have often heard such things as these: you are all troublesome comforters.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Shall windy words have no end? or is it any trouble to thee to speak?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 I also could speak like you: and would God your soul were for my soul. I would comfort you also with words, and would wag my head over you.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 I would strengthen you with my mouth, and would move my lips, as sparing you.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 But what shall I do? If I speak, my pain will not rest: and if I hold my peace, it will not depart from me.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 But now my sorrow hath oppressed me, and all my limbs are brought to nothing.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 My wrinkles bear witness against me, and a false speaker riseth up against my face, contradicting me.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 He hath gathered together his fury against me, and threatening me he hath gnashed with his teeth upon me: my enemy hath beheld me with terrible eyes.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 They have opened their mouths upon me, and reproaching me they have struck me on the cheek, they are filled with my pains.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 God hath shut me up with the unjust man, and hath delivered me into the hands of the wicked.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 I that was formerly so wealthy, am all on a sudden broken to pieces: he hath taken me by my neck, he hath broken me, and hath set me up to be his mark.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 He hath compassed me round about with his lances, he hath wounded my loins, he hath not spared, and hath poured out my bowels on the earth.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 He hath torn me with wound upon wound, he hath rushed in upon me like a giant.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 I have sowed sackcloth upon my skin, and have covered my flesh with ashes.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 My face is swollen with weeping, and my eyelids are dim.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 These things have I suffered without the iniquity of my hand, when I offered pure prayers to God.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 O earth, cover not thou my blood, neither let my cry find a hiding place in thee.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 For behold my witness is in heaven, and he that knoweth my conscience is on high.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 My friends are full of words: my eye poureth out tears to God.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 And O that a man might so be judged with God, as the son of man is judged with his companion!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 For behold short years pass away and I am walking in a path by which I shall not return.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >