< Job 10 >

1 My soul is weary of my life, I will let go my speech against myself, I will speak in the bitterness of my soul.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 I will say to God: Do not condemn me: tell me why thou judgest me so.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Doth it seem good to thee that thou shouldst calumniate me, and oppress me, the work of thy own hands, and help the counsel of the wicked?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Hast thou eyes of flesh: or, shalt thou see as man seeth?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Are thy days as the days of man, and are thy years as the times of men:
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 That thou shouldst inquire after my iniquity, and search after my sin?
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 And shouldst know that I have done no wicked thing, whereas there is no man that can deliver out of thy hand.
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Thy hands have made me, and fashioned me wholly round about, and dost thou thus cast me down headlong on a sudden?
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Remember, I beseech thee, that thou hast made me as the clay, and thou wilt bring me into dust again.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Hast thou not milked me as milk, and curdled me like cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Thou hast clothed me with skin and flesh: thou hast put me together with bones and sinews:
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Thou hast granted me life and mercy, and thy visitation hath preserved my spirit.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Although thou conceal these things in thy heart, yet I know that thou rememberest all things.
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 If I have sinned and thou hast spared me for an hour: why dost thou not suffer me to be clean from my iniquity?
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 And if I be wicked, woe unto me: and if just, I shall not lift up my head, being filled with affliction and misery.
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 And for pride thou wilt take me as a lioness, and returning thou tormentest me wonderfully.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Thou renewest thy witnesses against me, and multipliest thy wrath upon me, and pains war against me.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Why didst thou bring me forth out of the womb: O that I had been consumed that eye might not see me!
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 I should have been as if I had not been, carried from the womb to the grave.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Shall not the fewness of my days be ended shortly? suffer me, therefore, that I may lament my sorrow a little:
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 Before I go, and return no more, to a land that is dark and covered with the mist of death:
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 A land of misery and darkness, where the shadow of death, and no order, but everlasting horror dwelleth.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >