< Jeremiah 9 >

1 Who will give water to my head, and a fountain of tears to my eyes? and I will weep day and night for the slain of the daughter of my people.
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Who will give me in the wilderness a lodging place of wayfaring men, and I will leave my people, and depart from them? because they are all adulterers, an assembly of transgressors.
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 And they have bent their tongue, as a bow, for lies, and not for truth: they have strengthened themselves upon the earth, for they have proceeded from evil to evil, and me they have not known, saith the Lord.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Let every man take heed of his neighbor, and let his not trust in any brother of his: for every brother will utterly supplant, and every friend will walk deceitfully.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 And a man shall mock his brother, and they will not speak the truth: for they have taught their tongue to speak lies: they have laboured to commit iniquity.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Thy habitation is in the midst of deceit: Through deceit they have refused to know me, saith the Lord.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Therefore thus saith the Lord of hosts: Behold I will melt, and try them: for what else shall I do before the daughter of my people?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Their tongue is a piercing arrow, it hath spoken deceit: with his mouth one speaketh peace with his friend, and secretly he lieth in wait for him.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Shall I not visit them for these things, saith the Lord? or shall not my soul be revenged on such a nation?
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 For the mountains I will take up weeping and lamentation, and for the beautiful places of the desert, mourning: because they are burnt up, for that there is not a man that passeth through them: and they have not heard the voice of the owner: from the fowl of the air to the beasts they are gone away and departed.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 And I will make Jerusalem to be heaps of sand, and dens of dragons: and I will make the cities of Juda desolate, for want of an inhabitant.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Who is the wise man, that may understand this, and to whom the word of the mouth of the Lord may come that he may declare this, why the land hath perished, and is burnt up like a wilderness, which none passeth through?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 And the Lord said: Because they have forsaken my law, which I gave them, and have not heard my voice, and have not walked in it.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 But they have gone after the perverseness of their own heart, and after Baalim, which their fathers taught them.
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 Therefore thus saith the Lord of hosts the God of Israel: Behold I will feed this people with wormwood, and give them water of gall to drink.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 And I will scatter them among the nations, which they and their fathers have not known: and I will send the sword after them till they be consumed.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Thus saith the Lord of hosts the God of Israel: Consider ye, and call for the mourning women, and let them come: and send to them that are wise women, and let them make haste:
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Let them hasten and take up a lamentation for us: let our eyes shed tears, and our eyelids run down with waters.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 For a voice of wailing is heard out of Sion: How are we wasted and greatly confounded? because we have left the land, because our dwellings are cast down.
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Hear therefore, ye women, the word of the Lord: and let your ears receive the word of his mouth: and teach your daughters wailing: and every one her neighbor mourning.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 For death is come up through our windows, it is entered into our houses to destroy the children from without, the young men from the streets.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Speak: Thus saith the Lord: Even the carcass of man shall fall as dung upon the face of the country, and as grass behind the back of the mower, and there is none to gather it.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Thus saith the Lord: Let not the wise man glory in his wisdom, and let not the strong man glory in his strength, and let not the rich man glory in his riches:
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 But let him that glorieth glory in this, that he understandeth and knoweth me, for I am the Lord that exercise mercy, and judgment, and justice in the earth: for these things please me, saith the Lord.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Behold, the days come, saith the Lord, and I will visit upon every one that hath the foreskin circumcised.
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 Upon Egypt, and upon Juda, and upon Edom, and upon the children of Ammon, and upon Moab, and upon all that have their hair polled round, that dwell in the desert: for all the nations are uncircumcised in the flesh, but all the house of Israel are uncircumcised in the heart.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremiah 9 >