< Jeremiah 8 >
1 At that time, saith the Lord, they shall cast out the bones of the kings of Juda, and the bones of the princes thereof, and the bones of the priests, and the bones of the inhabitants of Jerusalem, out of their graves.
Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
2 And they shall spread them abroad to the sun, and the moon, and all the host of heaven, whom they have loved, and whom they have served, and after whom they have walked, and whom they have sought, and adored: they shall not be gathered, and they shall not be buried: they shall be as dung upon the face of the earth.
Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
3 And death shall be chosen rather than life by all that shall remain of this wicked kindred in all places, which are left, to which I have cast them out, saith the Lord of hosts.
Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
4 And thou shalt say to them: Thus saith the Lord: Shall not he that falleth, rise again? and he that is turned away, shall he not turn again?
“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
5 Why then is this people in Jerusalem turned away with a stubborn revolting? they have laid hold on lying, and have refused to return.
Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
6 I attended, and hearkened; no man speaketh what is good, there is none that doth penance for his sin, saying: What have I done? They are all turned to their own course, as a horse rushing to the battle.
Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
7 The kite in the air hath known her time: the turtle, and the swallow, and the stork have observed the time of their coming: but my people have not known the judgment of the Lord.
Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
8 How do you say: We are wise, and the law of the Lord is with us? Indeed the lying pen of the scribes hath wrought falsehood.
“‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
9 The wise men are confounded, they are dismayed, and taken: for they have cast away the word of the Lord, and there is no wisdom in them.
Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
10 Therefore I will give their women to strangers, their fields to others for an inheritance: because from the least even to the greatest all follow covetousness: from the prophet even to the priest, all deal deceitfully.
Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
11 And they healed the breach of the daughter of my people disgracefully, saying Peace, peace: when there was no peace.
Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
12 They are confounded, because they have committed abomination: yea rather they are not confounded with confusion, and they have not know how to blush: therefore shall they fall among them that fall; in the time of their visitation they shall fall, saith the Lord.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
13 Gathering I will gather them together, saith the Lord, there is no grape on the vines, and there are no figs on the fig tree, the leaf is fallen: and I have given them the things that are passed away.
“‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
14 Why do we sit still? assemble yourselves, and let us enter into the fenced city, and let us be silent there: for the Lord our God hath put us to silence, and hath given us water of gall to drink: for we have sinned against the Lord.
Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
15 We looked for peace and no good came: for a time of healing, and behold fear.
Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 The snorting of his horse was heard from Dan, all the land was moved at the sound of the neighing of his warriors: and they came and devoured the land, and all that was in it: the city and its inhabitants.
Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
17 For behold I will send among you serpents, basilisks, against which there is no charm: and they shall bite you, saith the Lord.
Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
18 My sorrow is above sorrow, my heart mourneth within me.
Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
19 Behold the voice of the daughter my people from a far country: Is not the Lord in Sion, or is not her king in her? why then have they provoked me to wrath with their idols, and strange vanities?
Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
20 The harvest is passed, the summer is ended, and we are not saved.
“Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
21 For the affliction of the daughter of my people I am afflicted, and made sorrowful, astonishment hath taken hold on me.
Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 Is there no balm in Galaad? or is no physician there? Why then is not the wound of the daughter of my people closed?
Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?