< Jeremiah 51 >

1 Thus saith the Lord: Behold I will raise up as it were a pestilential wind against Babylon and against the inhabitants thereof, who have lifted up their heart against me.
Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
2 And I will send to Babylon fanners, and they shall fan her, and shall destroy her land: for they are come upon her on every side in the day of her affliction.
Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
3 Let not him that bendeth, bend his bow, and let not, him go up that is armed with a coat of mail: spare not her young men, destroy all her army.
Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
4 And the slain shall fall in the land of the Chaldeans, and the wounded in the regions thereof.
Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
5 For Israel and Juda have not been forsaken by their God the Lord of hosts: but their land hath been filled with sin against the Holy One of Israel.
Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
6 Flee ye from the midst of Babylon, and let every one save his own life: be not silent upon her iniquity: for it is the time of revenge from the Lord, he will I render unto her what she hath deserved.
“Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
7 Babylon hath been a golden cup in the hand of the Lord, that made all the earth drunk: the nations have drunk of her wine, and therefore they have staggered.
Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
8 Babylon is suddenly fallen, and destroyed: howl for her, take balm for her pain, if so she may be healed.
Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
9 We would have cured Babylon, but she is not healed: let us forsake her, and let us go every man to his own land: because her judgment hath reached even to the heavens, and is lifted up to the clouds.
Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
10 The Lord hath brought forth our justices: Come, and let us declare in Sion the work of the Lord our God.
“‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
11 Sharpen the arrows, fill the quivers, the Lord hath raised up the spirit of the kings of the Medes: and his mind is against Babylon to destroy it, because it is the vengeance of the Lord, the vengeance of his temple.
“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
12 Upon the walls of Babylon set up the standard, strengthen the watch: set up the watchmen, prepare the ambushes: for the Lord hath both purposed, and done all that he spoke against the inhabitants of Babylon.
Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
13 O thou that dwellest upon many waters, rich in treasures, thy end is come for thy entire destruction.
Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
14 The Lord of hosts hath sworn by himself, saying: I will fill thee with men as with locusts, and they shall lift up a joyful shout against thee.
Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
15 He that made the earth by his power, that hath prepared the world by his wisdom, and stretched out the heavens by his understanding.
“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
16 When he uttereth his voice the waters are multiplied in heaven: he lifteth up the clouds from the ends of the earth, he hath turned lightning into rain: and hath brought forth the wind out of his treasures.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
17 Every man is become foolish by his knowledge: every founder is confounded by his idol, for what he hath cast is a lie, and there is no breath in them.
“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
18 They are vain works, and worthy to be laughed at, in the time of their visitation they shall perish.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
19 The portion of Jacob is not like them: for he that made all things he it is, and Israel is the sceptre of his inheritance: the Lord of hosts is his name.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
20 Thou dashest together for me the weapons of war, and with thee I will dash nations together, and with thee I will destroy kingdoms:
“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
21 And with thee I will break in pieces the horse, and his rider, and with thee I will break in pieces the chariot, and him that getteth up into it:
ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
22 And with thee I will break in pieces man and woman, and with thee I will break in pieces the old man and the child, and with thee I will break in pieces the young man and the virgin:
Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
23 And with thee I will break in pieces the shepherd and his dock, and with thee I will break in pieces the husbandman and his yoke of oxen, and with thee I will break in pieces captains and rulers.
Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
24 And I will render to Babylon, and to all the inhabitants of Chaldea all their evil, that they have done in Sion, before your eyes, saith the Lord.
“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 Behold I come against thee, thou destroying mountain, saith the Lord, which corruptest the whole earth: and I will stretch out my hand upon thee, and will roll thee down from the rocks, and will make thee a burnt mountain.
“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
26 And they shall not take of thee a stone for the corner, nor a stone for foundations, but thou shalt be destroyed for ever, saith the Lord.
Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
27 Set ye up a standard in the land: sound with the trumpet among the nations: prepare the nations against her: call together against her the kings of Ararat, Menni, and Ascenez: number Taphsar against her, bring the horse as the stinging locust.
“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
28 Prepare the nations against her, the kings of Media, their captains, and all their rulers, and all the land of their dominion.
Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
29 And the land shall be in a commotion, and shall be troubled: for the design of the Lord against Babylon shall awake, to make the land of Babylon desert and uninhabitable.
Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
30 The valiant men of Babylon have forborne to fight, they have dwelt in holds: their strength hath failed, and they are become as women: her dwelling places are burnt, her bars are broken.
Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31 One running post shall meet another, and messenger shall meet messenger: to tell the king of Babylon that his city is taken from one end to the other:
Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
32 And that the fords are taken, and the marshes are burnt with fire, and the men of war are affrighted.
Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
33 For thus saith the Lord of hosts the God of Israel: The daughter of Babylon is like a thrashingfloor, this is the time of her thrashing: yet a little while, and the time of her harvest shall come.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
34 Nabuchodonosor king of Babylon hath eaten me up, he hath devoured me: he hath made me as an empty vessel: he hath swallowed me up like a dragon, he hath filled his belly with my delicate meats, and he hath cast me out.
A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
35 The wrong done to me, and my flesh be upon Babylon, saith the habitation of Sion: and my blood upon the inhabitants of Chaldea, saith Jerusalem.
Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
36 Therefore thus saith the Lord: Behold I will judge thy cause, and will take vengeance for thee, and I will make her sea desolate, and will dry up her spring.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
37 And Babylon shall be reduced to heaps, a dwelling place for dragons, an astonishment and a hissing, because there is no inhabitant.
Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
38 They shall roar together like lions, they shall shake their manes like young lions.
Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
39 In their heat I will set them drink: and I will make them drunk, that they may slumber, and sleep an everlasting sleep, and awake no more, saith the Lord.
Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
40 I will bring them down like lambs to the slaughter, and like rams with kids.
“Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
41 How is Sesach taken, and the renowned one of all the earth surprised? How is Babylon become an astonishment among the nations?
“Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
42 The sea is come up over Babylon: she is covered with the multitude of the waves thereof.
Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
43 Her cities are become an astonishment, a land uninhabited and desolate, a land wherein none can dwell, nor son of man pass through it.
Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
44 And I will visit against Bel in Babylon, and I will bring forth out of his mouth that which he had swallowed down: and the rations shall no more flow together to him, for the wall also of Babylon shall fall.
Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
45 Go out of the midst of her, my people: that every man may save his life from the fierce wrath of the Lord.
“Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
46 And lest your hearts faint, and ye fear for the rumour that shall be heard in the land: and a rumour shall come in one year, and after this year another rumour: and iniquity in the land, and ruler upon ruler.
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
47 Therefore behold the days come, and I will visit the idols of Babylon: and her whole land shall be confounded, and all her slain shall fall in the midst of her.
Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
48 And the heavens and the earth, and all things that are in them shall give praise for Babylon: for spoilers shall come to her from the north, saith the Lord.
Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
49 And as Babylon caused that there should fall slain in Israel: so of Babylon there shall fall slain in all the earth.
“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
50 You that have escaped the sword, come away, stand not still: remember the Lord afar off, and let Jerusalem come into your mind.
Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
51 We are confounded, because we have heard reproach: shame hath covered our faces: because strangers are come upon the sanctuaries of the house of the Lord.
Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
52 Therefore behold the days come, saith the Lord, and I will visit her graven things, and in all her land the wounded shall groan:
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
53 If Babylon should mount up to heaven, and establish her strength on high: from me there should come spoilers upon her, saith the Lord.
Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
54 The noise of a cry from Babylon, and great destruction from the land of the Chaldeans:
“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
55 Because the Lord hath laid Babylon waste, and destroyed out of her the great voice: and their wave shall roar like many waters: their voice hath made a noise:
Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
56 Because the spoiler is come upon her, that is, upon Babylon, and her valiant men are taken, and their bow is weakened, because the Lord, who is a strong revenger, will surely repay.
Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
57 And I will make her princes drunk. and her wise men, and her captains, and her rulers, and her valiant men: and they shall sleep an everlasting sleep, and shall awake no more, saith the whose name is Lord of hosts.
Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
58 Thus saith the Lord of hosts: That broad wall of Babylon shall be utterly broken down, and her high gates shall be burnt with fire, and the labours of the people shall come to nothing, and of the nations shall go to the fire, and shall perish.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
59 The word that Jeremias the prophet commanded Saraias the son of Nerias, the son of Maasias, when he went with king Sedecias to Babylon, in the fourth year of his reign: now Saraias was chief over the prophecy.
Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 And Jeremias wrote in one book all the evil that was to come upon Babylon: all these words that are written against Babylon.
Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 And Jeremias said to Saraias: When thou shalt come into Babylon, and shalt see, and shalt read all these words,
Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 Thou shalt say: O Lord, thou hast spoken against this place to destroy it: so that there should be neither man nor beast to dwell therein, and that it should be desolate for ever.
Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 And when thou shalt have made an end of reading this book, thou shalt tie a stone to it, and shalt throw it into the midst of the Euphrates:
Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 And thou shalt say: Thus shall Babylon sink, and she shall not rise up from the affliction that I will bring upon her, and she shall be utterly destroyed. Thus far are the words of Jeremias.
Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

< Jeremiah 51 >