< Isaiah 44 >

1 And now hear, O Jacob, my servant, and Israel whom I have chosen.
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Thus saith the Lord that made and formed thee, thy helper from the womb: Fear not, O my servant Jacob, and thou most righteous whom I have chosen.
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 For I will pour out waters upon the thirsty ground, and streams upon the dry land: I will pour out my spirit upon thy seed, and my blessing upon thy stock.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 And they shall spring up among the herbs, as willows beside the running waters.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 One shall say: I am the Lord’s, and another shall call himself by the name of Jacob, and another shall subscribe with his hand, To the Lord, and surname himself by the name of Israel.
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 Thus saith the Lord the king of Israel, and his redeemer the Lord of hosts: I am the brat, and I am the last, and besides me there is no God.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Who is like to me? let him call and declare: and let him set before me the order, since I appointed the ancient people: and the things to come, and that shall be hereafter, let them shew unto them.
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Fear ye not, neither be ye troubled, from that time I have made thee to hear, and have declared: you are my witnesses. Is there a God besides me, a maker, whom I have not known?
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 The makers of idols are all of them nothing, and their best beloved things shall not profit them. They are their witnesses, that they do not see, nor understand, that they may be ashamed.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Who hath formed a god, and made a graven thing that is profitable for nothing?
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Behold, all the partakers thereof shall be confounded: for the makers are men: they shall all assemble together, they shall stand and fear, and shall be confounded together.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 The smith hath wrought with his file, with coals, and with hammers he hath formed it, and hath wrought with the strength of his arm: he shall hunger and faint, he shall drink no water, and shall be weary.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 The carpenter hath stretched out his rule, he hath formed it with a plane: he hath made it with corners, and hath fashioned it round with the compass: and he hath made the image of a man as it were a beautiful man dwelling in a house.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 He hath cut down cedars, taken the holm, and the oak that stood among the trees of the forest: he hath planted the pine tree, which the rain hath nourished.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 And it hath served men for fuel: he took thereof, and warmed himself: and he kindled it, and baked bread: but of the rest he made a god, and adored it: he made a graven thing, and bowed down before it.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Part of it he burnt with fire, and with part of it he dressed his meat: he boiled pottage, and was filled, and was warmed, and said: Aha, I am warm, I have seen the fire.
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 But the residue thereof he made a god, and a graven thing for himself: he boweth down before it, and adoreth it, and prayeth unto it, saying: Deliver me, for thou art my God.
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 They have not known, nor understood: for their eyes are covered that they may not see, and that they may not understand with their heart.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 They do not consider in their mind, nor know, nor have the thought to say: I have burnt part of it in the fire, and I have baked bread upon the coals thereof: I have broiled flesh and have eaten, and of the residue thereof shall I make an idol? shall I fall down before the stock of a tree?
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Part thereof is ashes: his foolish heart adoreth it, and he will not save his soul, nor say: Perhaps there is a lie in my right hand.
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 Remember these things, O Jacob, and Israel, for thou art my servant. I have formed thee, thou art my servant, O Israel, forget me not.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 I have blotted out thy iniquities as a cloud, and thy sins as a mist: return to me, for I have redeemed thee.
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 Give praise, O ye heavens, for the Lord hath shewn mercy: shout with joy, ye ends of the earth: ye mountains, resound with praise, thou, O forest, and every tree therein: for the Lord hath redeemed Jacob, and Israel shall be glorified.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Thus saith the Lord thy redeemer, and thy maker, from the womb: I am the Lord, that make all things, that alone stretch out the heavens, that establish the earth, and there is none with me.
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 That make void the tokens of diviners, and make the soothsayers mad. That turn the wise backward, and that, make their knowledge foolish.
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 That raise up the word of my servant and perform the counsel of my messengers, who say to Jerusalem: Thou shalt be inhabited: and to the cities of Juda: You shall be built, and I will raise up the wastes thereof.
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 Who say to the deep: Be thou desolate, and I will dry up thy rivers.
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 Who say to Cyrus: Thou art my shepherd, and thou shalt perform all my pleasure. Who say to Jerusalem: Thou shalt be built: and to the temple: Thy foundations shall be laid.
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”

< Isaiah 44 >