< Isaiah 27 >

1 In that day the Lord with his hard, and great, and strong sword shall visit leviathan the bar serpent, and leviathan the crooked serpent, and shall slay the whale that is in the see.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 In that day there shall be singing to the vineyard of pure wine.
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 I am the Lord that keep it, I will suddenly give it drink: lest any hurt come to it, I keep it night and day.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 There is no indignation in me: who shall make me a thorn and a brier in battle: shall march against it, shall I set it on fire together?
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Or rather shall it take hold of my strength, shall it make peace with me, shall it make peace with me?
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 When they shall rush in unto Jacob, Israel shall blossom and bud, and they shall fill the face of the world with seed.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Hath he struck him according to the stroke of him that struck him? or is he slain, as he killed them that were slain by him?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 In measure against measure, when it shall be cast off, thou shalt judge it. He hath meditated with his severe spirit in the day of heat.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Therefore upon this shall the iniquity of the house of Jacob be forgiven: and this is all the fruit, that the sin thereof should be taken away, when he shall have made all the stones of the altar, as burnt stones broken in pieces, the groves and temples shall not stand.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 For the strong city shall be desolate, the beautiful city shall be forsaken, and shall be left as a wilderness: there the calf shall feed, and there shall he lie down, and shall consume its branches.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Its harvest shall be destroyed with drought, women shall come and teach it: for it is not a wise people, therefore he that made it, shall not have mercy on it: and he that formed it, shall not spare it.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 And it shall come to pass, that in that day the Lord will strike from the channel of the river even to the torrent of Egypt, and you shall be gathered together one by one, O ye children of Israel.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 And it shall come to pass, that in that day a noise shall be made with a great trumpet, and they that were lost, shall come from the land of the Assyrians, and they that were outcasts in the land of Egypt, and they shall adore the Lord in the holy mount in Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

< Isaiah 27 >