< Deuteronomy 31 >

1 And Moses went, and spoke all these words to all Israel,
Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
2 And he said to them: I am this day a hundred and twenty years old, I can no longer go out and come in, especially as the Lord also hath said to me: O Thou shalt not pass over this Jordan.
“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
3 The Lord thy God then will pass over before thee: he will destroy all these nations in thy sight, and thou shalt possess them: and this Josue shall go over before thee, as the Lord hath spoken.
Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
4 And the Lord shall do to them as he did to Sehon and Og the kings of the Amorrhites, and to their land, and shall destroy them.
Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
5 Therefore when the Lord shall have delivered these also to you, you shall do in like manner to them as I have commanded you,
Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
6 Do manfully and be of good heart: fear not, nor be ye dismayed at their sight: for the Lord thy God he himself is thy leader, and will not leave thee nor forsake thee.
Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
7 And Moses called Josue, and said to him before all Israel: Take courage, and be valiant: for thou shalt bring this people into the land which the Lord swore he would give to their fathers, and thou shalt divide it by lot.
Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
8 And the Lord who is your leader, he himself will be with thee: he will not leave thee, nor forsake thee: fear not, neither be dismayed.
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
9 And Moses wrote this law, and delivered it to the priests the sons of Levi, who carried the ark of the covenant of the Lord, and to all the ancients of Israel.
Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
10 And he commanded them, saying: After seven years, in the year of remission, in the feast of tabernacles,
Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
11 When all Israel come together, to appear in the sight of the Lord thy God in the place which the Lord shall choose, thou shalt read the words of this law before all Israel, in their hearing,
pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
12 And the people being all assembled together, both men and women, children and strangers, that are within thy gates: that hearing they may learn, and fear the Lord your God, and keep, and fulfill all the words of this law:
Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
13 That their children also, who now are ignorant, may hear, and fear the Lord their God, all the days that they lire in the land whither you are going over the Jordan to possess it.
Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
14 And the Lord said to Moses: Behold the days of thy death are nigh: call Josue, and stand ye in the tabernacle of the testimony, that I may give him a charge. So Moses and Josue went and stood in the tabernacle of the testimony:
Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
15 And the Lord appeared there in the pillar of a cloud, which stood in the entry of the tabernacle.
Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
16 And the Lord said to Moses: Behold thou shalt sleep with thy fathers, and this people rising up will go a fornicating after strange gods in the land, to which it goeth in to dwell: there will they forsake me, and will make void the covenant, which I have made with them,
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
17 And my wrath shall be kindled against them in that day: and I will forsake them, and will hide my face from them, and they shall be devoured: all evils and afflictions shall find them, so that they shall say in that day: In truth it is because God is not with me, that these evils have found me.
Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
18 But I will hide, and cover my face in that day, for all the evils which they have done, because they have followed strange gods.
Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
19 Now therefore write you this canticle, and teach the children of Israel: that they may know it by heart, and sing it by mouth, and this song may be unto me for a testimony among the children of Israel.
“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
20 For I will bring them into the land, for which I swore to their fathers, that floweth with milk and honey. And when they have eaten, and are full and fat, they will turn away after strange gods, and will serve them: and will despise me, and make void my covenant.
Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
21 And after many evils and afflictions shall have come upon them, this canticle shall answer them for a testimony, which no oblivion shall take away out of the mouth of their seed. For I know their thoughts, and what they are about to do this day, before that I bring them into the land which I have promised them.
Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
22 Moses therefore wrote the canticle and taught it to the children of Israel.
Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
23 And the Lord commanded Josue the son of Nun, and said: Take courage, and be valiant: for thou shalt bring the children of Israel into the land which I have promised, and I will be with thee.
Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
24 Therefore after Moses had wrote the words of this law in a volume, and finished it:
Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
25 He commanded the Levites, who carried the ark of the covenant of the Lord. saying:
analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
26 Take this book, and put it in the side of the ark of the covenant of the Lord your God: that it may be there for a testimony against thee.
“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
27 For I know thy obstinacy, and thy most stiff neck, While I am yet living, and going in with you, you have always been rebellious against the Lord: how much more when I shall be dead?
Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
28 Gather unto me all the ancients of your tribes, and your doctors, and I will speak these words in their hearing, and will call heaven and earth to witness against them.
Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
29 For I know that, after my death, you will do wickedly, and will quickly turn aside from the way that I have commanded you: and evils shall come upon you in the latter times, when you shall do evil in the sight of the Lord, to provoke him by the works of your hands.
Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
30 Moses therefore spoke, in the hearing of the whole assembly of Israel, the words of this canticle, and finished it even to the end,
Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:

< Deuteronomy 31 >