< 2 Samuel 22 >

1 And David spoke to the Lord the words of this canticle, in the day that the Lord delivered him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul,
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 And he said: The Lord is my rock, and my strength, and my saviour.
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 God is my strong one, in him will I trust: my shield, and the horn of my salvation: he lifteth me up, and is my refuge: my saviour, thou wilt deliver me from iniquity.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 I will call on the Lord who is worthy to be praised: and I shall be saved from my enemies.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 For the pangs of death have surrounded me: the floods of Belial have made me afraid.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 The cords of hell compassed me: the snares of death prevented me. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 In my distress I will call upon the Lord, and I will cry to my God: and he will hear my voice out of his temple, and my cry shall come to his ears.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 The earth shook and trembled, the foundations of the mountains were moved, and shaken, because he was angry with them.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 A smoke went up from his nostrils, and a devouring fire out of his mouth: coals were kindled by it.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 He bowed the heavens, and came down: and darkness was under his feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 And he rode upon the cherubims, and flew: and slid upon the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 He made darkness a covering round about him: dropping waters out of the clouds of the heavens.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 By the brightness before him, the coals of fire were kindled.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 The Lord shall thunder from heaven: and the most high shall give forth his voice.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 He shot arrows and scattered them: lightning, and consumed them.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 And the overflowings of the sea appeared, and the foundations of the world were laid open at the rebuke of the Lord, at the blast of the spirit of his wrath.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 He sent from on high, and took me, and drew me out of many waters.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 He delivered me from my most mighty enemy, and from them that hated me: for they were too strong for me.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 He prevented me in the day of my affliction, and the Lord became my stay.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 And he brought me forth into a large place, he delivered me, because I pleased him.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 The Lord will reward me according to my justice: and according to the cleanness of my hands he will render to me.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Because I have kept the ways of the Lord, and have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 For all his judgments are in my sight: and his precepts I have not removed from me.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 And I shall be perfect with him: and shall keep myself from my iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 And the Lord will recompense me according to my justice: and according to the cleanness of my hands in the sight of his eyes.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 With the holy one thou wilt be holy: and with the valiant perfect.
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 With the elect thou wilt be elect: and with the perverse thou wilt be perverted.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 And the poor people thou wilt save: and with thy eyes thou wilt humble the haughty.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 For thou art my lamp, O Lord: and thou, O Lord, wilt enlighten my darkness.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 For in thee I will run girded: in my God I will leap over the wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 God, his way is immaculate, the word of the Lord is tried by fire: he is the shield of all that trust in him.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Who is God but the Lord: and who is strong but our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 God who hath girded me with strength, and made my way perfect.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Making my feet like the feet of harts, and setting me upon my high places.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 He teacheth my bands to war: and maketh my arms like a bow of brass.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Thou hast given me the shield of my salvation: and thy mildness hath multiplied me.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Thou shalt enlarge my steps under me: and my ankles shall not fail.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 I will pursue after my enemies, and crush them: and will not return again till I consume them.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 I will consume them and break them in pieces, so that they shall not rise: they shall fall under my feet.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Thou hast girded me with strength to battle: thou hast made them that resisted me to bow under me.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 My enemies thou hast made to turn their back to me: them that hated me, and I shall destroy them.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 They shall cry, and there shall be none to save: to the Lord, and he shall not hear them.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 I shall beat them as small as the dust of the earth: I shall crush them and spread them abroad like the mire of the streets.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 Thou wilt save me from the contradictions of my people: thou wilt keep me to be the head of the Gentiles: the people which I know not, shall serve me,
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 The sons of the stranger will resist me, at the hearing of the ear they will obey me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 The strangers are melted away, and shall be straitened in their distresses.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 The Lord liveth, and my God is blessed: and the strong God of my salvation shall be exalted:
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 God who giveth me revenge, and bringest down people under me,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 Who bringest me forth from my enemies, and liftest me up from them that resist me: from the wicked man thou shalt deliver me.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Therefore will I give thanks to thee. O Lord, among the Gentiles, and will sing to thy name.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 Giving great salvation to his king, and shewing mercy to David his anointed, and to his seed for ever.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >