< 2 Kings 25 >
1 And it came to pass in the ninth year of his reign, in the tenth month, the tenth day of the month, that Nabuchodonosor king of Babylon came, he and all his army against Jerusalem: and they surrounded it: and raised works round about it.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 And the city was shut up and besieged till the eleventh year of king Sedecias,
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 The ninth day of the month: and a famine prevailed in the city, and there was no bread for the people of the land.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 And a breach was made into the city: and all the men of war fled in the night between the two walls by the king’s garden, (now the Chaldees besieged the city round about, ) and Sedecias fled by the way that leadeth to the plains of the wilderness.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 And the army of the Chaldees pursued after the king, and overtook him in the plains of Jericho: and all the warriors that were with him were scattered, and left him:
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 So they took the king, and brought him to the king of Babylon to Reblatha, and he gave judgment upon him.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 And he slew the sons of Sedecias before his face, and he put out his eyes, and bound him with chains, and brought him to Babylon.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 In the fifth month, the seventh day of the month, that is, the nineteenth year of the king of Babylon, came Nabuzardan commander of the army, a servant of the king of Babylon, into Jerusalem.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 And he burnt the house of the Lord, and the king’s house, and the houses of Jerusalem, and every house he burnt with fire.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 And all the army of the Chaldees, which was with the commander of the troops, broke down the walls of Jerusalem round about.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 And Nabuzardan the commander of the army, carried away the rest of the people that remained in the city, and the fugitives that had gone over to the king of Babylon, and the remnant of the common people.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 But of the poor of the land he left some dressers of vines and husbandmen.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 And the pillars of brass that were in the temple of the Lord, and the bases, and the sea of brass which was in the house of the Lord, the Chaldees broke in pieces, and carried all the brass of them to Babylon.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 They took away also the pots of brass, and the mazers, and the forks, and the cups, and the mortars, and all the vessels of brass with which they ministered.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 Moreover also the censers, and the bowls, such as were of gold in gold, and such as were of silver in silver, the general of the army took away.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 That is, two pillars, one sea, and the bases which Solomon had made in the temple of the Lord: the brass of all these vessels was without weight.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 One pillar was eighteen cubits high, and the chapiter of brass which was upon it was three cubits high: and the network, and the pomegranates that were upon the chapiter of the pillar, were all of brass: and the second pillar had the like adorning.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 And the general of the army took Seraias the chief priest, and Sophonias the second priest, and three doorkeepers.
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 And out of the city one eunuch, who was captain over the men of war: and five men of them that had stood before the king, whom he found in the city, and Sopher the captain of the army who exercised the young soldiers of the people of the land: and threescore men of the common people, who were found in the city.
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 These Nabuzardan the general of the army took away, and carried them to the king of Babylon to Reblatha.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 And the king of Babylon smote them, and slew them at Reblatha in the land of Emath: so Juda was carried away out of their land.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 But over the people that remained in the land of Juda, which Nabuchodonosor king of Babylon had left, he gave the government to Godolias the son of Ahicam the son of Saphan.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 And when all the captains of the soldiers had heard this, they and the men that were with them, to wit, that the king of Babylon had made Godolias governor, they came to Godolias to Maspha, Ismael the son of Nathanias, and Johanan the son of Caree, and Saraia the son of Thanehumeth the Netophathite, and Jezonias the son of Maachathi, they and their men.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 And Godolias swore to them and to their men, saying: Be not afraid to serve the Chaldees: stay in the land, and serve the king of Babylon, and it shall be well with you.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 But it came to pass in the seventh month, that Ismael the son of Nathanias, the son of Elisama of the seed royal came, and ten men with him: and smote Godolias so that he died: and also the Jews and the Chaldees that were with him in Maspha.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 And all the people both little and great, and the captains of the soldiers, rising up went to Egypt, fearing the Chaldees.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 And it came to pass in the seven and thirtieth year of the captivity of Joachin king of Juda, in the twelfth month the seven and twentieth day of the month: Evilmerodach king of Babylon, in the year that he began to reign, lifted up the head of Joachin king of Juda out of prison.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 And he spoke kindly to him: and he set his throne above the throne of the kings that were with him in Babylon.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 And he changed his garments which he had in prison, and he ate bread always before him, all the days of his life.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 And he appointed him a continual allowance, which was also given him by the king day by day, all the days of his life.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.