< 2 Chronicles 28 >

1 Achaz was twenty years old when he began to reign, and he reigned sixteen years in Jerusalem: he did not that which was right in the sight of the Lord as David his father had done,
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 But walked in the ways of the kings of Israel; moreover also he cast statues for Baalim.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 It was he that burnt incense in the valley of Benennom, and consecrated his sons in the fire according to the manner of the nations, which the Lord slew at the coming of the children of Israel.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 He sacrificed also, and burnt incense in the high places, and on the hills, and under every green tree.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 And the Lord his God delivered him into the hands of the king of Syria, who defeated him, and took a great booty out of his kingdom, and carried it to Damascus: he was also delivered into the hands of the king of Israel, who overthrew him with a great slaughter.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 For Phacee the son of Romelia slew of Juda a hundred and twenty thousand in one day, all valiant men: because they had forsaken the Lord the God of their fathers.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 At the same time Zechri a powerful man of Ephraim, slew Maasias the king’s son, and Ezricam the governor of his house, and Elcana who was next to the king.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 And the children of Israel carried away of their brethren two hundred thousand women, boys, and girls, and an immense booty: and they brought it to Samaria.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 At that time there was a prophet of the Lord there, whose name was Oded: and he went out to meet the army that came to Samaria, and said to them: Behold the Lord the God of your fathers being angry with Juda, hath delivered them into your hands, and you have butchered them cruelly, so that your cruelty hath reached up to heaven.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 Moreover you have a mind to keep under the children of Juda and Jerusalem for your bondmen and bondwomen, which ought not to be done: for you have sinned in this against the Lord your God.
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 But hear ye my counsel, and release the captives that you have brought of your brethren, because a great indignation of the Lord hangeth over you.
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 Then some of the chief men of the sons of Ephraim, Azarias the son of Johanan, Barachias the son of Mosollamoth, Ezechias the son of Sellum, and Amasa the son of Adali, stood up against them that came from the war.
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 And they said to them: You shall not bring in the captives hither, lest we sin against the Lord. Why will you add to our sins, and heap up upon our former offences? for the sin is great, and the fierce anger of the Lord hangeth over Israel.
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 So the soldiers left the spoils, and all that they had taken, before the princes and all the multitude.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 And the men, whom we mentioned above, rose up and took the captives, and with the spoils clothed all them that were naked: and when they had clothed and shed them, and refreshed them with meat and drink, and anointed them because of their labour, and had taken care of them, they set such of them as could not walk, and were feeble, upon beasts, and brought them to Jericho the city of palm trees to their brethren, and they returned to Samaria.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 At that time king Achaz sent to the king of the Assyrians asking help.
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 And the Edomites came and slew many of Juda, and took a great booty.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 The Philistines also spread themselves among the cities of the plains, and to the south of Juda: and they took Bethsames, and Aialon, and Gaderoth, and Socho, and Thamnan, and Gamzo, with their villages, and they dwelt in them.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 For the Lord had humbled Juda because of Achaz the king of Juda, for he had stripped it of help, and had contemned the Lord.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 And he brought, against him Thelgathphalnasar king of the Assyrians, who also afflicted him, and plundered him without any resistance.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 And Achaz stripped the house of the Lord, and the house of the kings, and of the princes, and gave gifts to the king of the Assyrians, and yet it availed him nothing.
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 Moreover also in the time of his distress he increased contempt against the Lord: king Achaz himself by himself,
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 Sacrificed victims to the gods of Damascus that struck him, and he said: The gods of the kings of Syria help them, and I will appease them with victims, and they will help me; whereas on the contrary they were the ruin of him, and of all Israel.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 Then Achaz having taken away all the vessels of the house of God, and broken them, shut up the doors of the temple of God, and made himself altars in all the corners of Jerusalem.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 And in all the cities of Juda he built altars to burn frankincense, and he provoked the Lord the God of his fathers to wrath.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 But the rest of his acts, and all his works first and last are written in the book of the kings of Juda and Israel.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 And Achaz slept with his fathers, and they buried him in the city of Jerusalem: for they received him not into the sepulchres of the kings of Israel. And Ezechias his son reigned in his stead.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 28 >