< 2 Chronicles 24 >

1 Joas was seven years old when he began to reign: and he reigned forty years in Jerusalem: the name of his mother was Sebia of Bersabee.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 And he did that which is good before the Lord all the days of Joiada the priest.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 And Joiada took for him two wives, by whom he had sons and daughters.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 After this Joas had a mind to repair the house of the Lord.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 And he assembled the priests, and the Levites, and said to them: Go out to the cities of Juda, and gather of all Israel money to repair the temple of your God, from year to year: and do this with speed: but the Levites were negligent.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 And the king called Joiada the chief, and said to him: Why hast thou not taken care to oblige the Levites to bring in out of Juda and Jerusalem the money that was appointed by Moses the servant of the Lord for all the multitude of Israel to bring into the tabernacle of the testimony?
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 For that wicked woman Athalia, and her children have destroyed the house of God, and adorned the temple of Baal with all the things that had been dedicated in the temple of the Lord.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 And the king commanded, and they made a chest: and set it by the gate of the house of the Lord on the outside.
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 And they made a proclamation in Juda and Jerusalem, that every man should bring to the Lord the money which Moses the servant of God appointed for all Israel, in the desert.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 And all the princes, and all the people rejoiced: and going In they contributed and cast so much into the chest of the Lord, that it was filled.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 And when it was time to bring the chest before the king by the hands of the Levites, (for they saw there was much money, ) the king’s scribe, and he whom the high priest had appointed went in: and they poured out the money that was in the chest: and they carried back the chest to its place: and thus they did from day to day, and there was gathered an immense sum of money.
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 And the king and Joiada gave it to those who were over the works of the house of the Lord: but they hired with it stonecutters, and artificers of every kind of work to repair the house of the Lord: and such as wrought in iron and brass, to uphold what began to be falling.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 And the workmen were diligent, and the breach of the walls was closed up by their hands, and they set up the house of the Lord in its former state, and made it stand firm.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 And when they had finished all the works, they brought the rest of the money before the king and Joiada: and with it were made vessels for the temple for the ministry, and for holocausts and bowls, and other vessels of gold and silver: and holocausts were offered in the house of the Lord continually all the days of Joiada.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 But Joiada grew old and was full of days, and died when he was a hundred and thirty years old.
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 And they buried him in the city of David among the kings, because he had done good to Israel, and to his house.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 And after the death of Joiada, the princes of Juda went in, and worshipped the king: and he was soothed by their services and hearkened to them.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 And they forsook the temple of the Lord the God of their fathers, and served groves and idols, and wrath came upon Juda and Jerusalem for this sin.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 And he sent prophets to them to bring them back to the Lord, and they would not give ear when they testified against them.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 The spirit of God then came upon Zacharias the son of Joiada the priest, and he stood in the sight of the people, and said to them: Thus saith the Lord God: Why transgress you the commandment of the Lord which will not be for your good, and have forsaken the Lord, to make him forsake you?
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 And they gathered themselves together against him, and stoned him at the king’s commandment in the court of the house of the Lord.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 And king Joas did not remember the kindness that Joiada his father had done to him, but killed his son. And when he died, he said: The Lord see, and require it.
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 And when a year was come about, the army of Syria came up against him: and they came to Juda and Jerusalem, and killed all the princes of the people, and they sent all the spoils to the king of Damascus.
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 And whereas there came a very small number of the Syrians, the Lord delivered into their hands an infinite multitude, because they had forsaken the Lord the God of their fathers: and on Joas they executed shameful judgments.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 And departing they left him in diseases: and his servants rose up him, for revenge of the blood of the son of Joiada the priest, and they slew him in his bed, and he died: and they buried him in the city of David, but not in the sepulchres of the kings.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Now the men that conspired against him were Zabad the son of Semmaath an Ammonitess, and Jozabad the son of Semarith a Moabitess.
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 And concerning his sons, and the sum of money which was gathered under him, and the repairing the house of God; they are written more diligently in the book of kings: and Amasias his son reigned in his stead.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 24 >